< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Psalmus David. Exultate iusti in Domino: rectos decet collaudatio.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Confitemini Domino in cithara: in psalterio decem chordarum psallite illi.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Cantate ei canticum novum: bene psallite ei in vociferatione.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Quia rectum est verbum Domini, et omnia opera eius in fide.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Diligit misericordiam et iudicium: misericordia Domini plena est terra.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Verbo Domini cæli firmati sunt: et spiritu oris eius omnis virtus eorum.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Congregans sicut in utre aquas maris: ponens in thesauris abyssos.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Timeat Dominum omnis terra: ab eo autem commoveantur omnes inhabitantes orbem.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Quoniam ipse dixit, et facta sunt: ipse mandavit, et creata sunt.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Dominus dissipat consilia gentium: reprobat autem cogitationes populorum, et reprobat consilia principum.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Consilium autem Domini in æternum manet: cogitationes cordis eius in generatione et generationem.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Beata gens, cuius est Dominus, Deus eius: populus, quem elegit in hereditatem sibi.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
De cælo respexit Dominus: vidit omnes filios hominum.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
De præparato habitaculo suo respexit super omnes, qui habitant terram.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Qui finxit sigillatim corda eorum: qui intelligit omnia opera eorum.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Non salvatur rex per multam virtutem: et gigas non salvabitur in multitudine virtutis suæ.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Fallax equus ad salutem: in abundantia autem virtutis suæ non salvabitur.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Ecce oculi Domini super metuentes eum: et in eis, qui sperant super misericordia eius.
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
Ut eruat a morte animas eorum: et alat eos in fame.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Anima nostra sustinet Dominum: quoniam adiutor et protector noster est.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Quia in eo lætabitur cor nostrum: et in nomine sancto eius speravimus.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Fiat misericordia tua Domine super nos: quemadmodum speravimus in te.

< Masalimo 33 >