< Masalimo 32 >

1 Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
A psalm of David. A maschil. Blessed is the person whose transgression is forgiven, whose sin is covered.
2 Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
Blessed is the man to whom Yahweh reckons no guilt and in whose spirit there is no deceit.
3 Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
When I remained silent, my bones were wasting away while I groaned all day long.
4 Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
For day and night your hand was heavy upon me. My strength withered as in summer drought. (Selah)
5 Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
Then I acknowledged my sin to you, and I no longer hid my iniquity. I said, “I will confess my transgressions to Yahweh,” and you forgave the guilt of my sin. (Selah)
6 Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
Because of this, all who are godly should pray to you at a time of great distress. Then when the surging waters overflow, they will not reach those people.
7 Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
You are my hiding place; you will guard me from trouble. You will surround me with the songs of victory. (Selah)
8 Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
I will instruct you and teach you in the way which you should go. I will instruct you with my eye upon you.
9 Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
Do not be like a horse or like a mule, which have no understanding; it is only with bridle and bit to control them that they will go where you want them to.
10 Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
The wicked have many sorrows, but Yahweh's covenant faithfulness will surround the one who trusts in him.
11 Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
Be glad in Yahweh, and rejoice, you righteous; shout for joy, all you who are upright in heart.

< Masalimo 32 >