< Masalimo 31 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
U tebe se, Gospode, uzdam; nemoj me ostaviti pod sramotom dovijeka, po pravdi svojoj izbavi me.
2 Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
Prigni k meni uho svoje, pohitaj, pomozi mi. Budi mi kameni grad, tvrda ograda, gdje bih se spasao.
3 Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
Jer si ti kamena gora moja i ograda moja, imena svojega radi vodi me i upravljaj mnom.
4 Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
Izvadi me iz mreže, koju mi tajno zamjestiše; jer si ti krjepost moja.
5 Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
U tvoju ruku predajem duh svoj; izbavljao si me, Gospode, Bože istini!
6 Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
Nenavidim one koji poštuju propadljive idole; ja se u Gospoda uzdam.
7 Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
Radovaæu se i veseliti se o milosti tvojoj, kad pogledaš na moju muku, poznaš tugu duše moje,
8 Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
Ne daš me u ruku neprijatelju, postaviš noge moje na prostranom mjestu.
9 Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
Smiluj se na me, Gospode; jer me je tuga, od jada iznemože oko moje, duša moja i srce moje.
10 Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
Išèilje u žalosti život moj, i godine moje u uzdisanju; oslabi od muke krjepost moja, i kosti moje sasahnuše.
11 Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
Od množine neprijatelja svojih postadoh potsmijeh i susjedima svojim, i strašilo znancima svojim; koji me vide na ulici, bježe od mene.
12 Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
Zaboravljen sam kao mrtav, nema me u srcima; ja sam kao razbijen sud.
13 Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
Jer slušam grdnju od mnogih, otsvuda strah, kad se dogovaraju na me, misle išèupati dušu moju.
14 Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
A ja se, Gospode, u tebe uzdam i velim: ti si Bog moj.
15 Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
U tvojoj su ruci dani moji; otmi me iz ruku neprijatelja mojijeh, i od onijeh, koji me gone.
16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
Pokaži svijetlo lice svoje sluzi svojemu; spasi me milošæu svojom.
17 Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol h7585)
Gospode! nemoj me ostaviti pod sramotom; jer tebe prizivljem. Nek se posrame bezbožnici, neka zamuknu i padnu u pakao. (Sheol h7585)
18 Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
Neka onijeme usta lažljiva, koja govore na pravednika obijesno, oholo i s porugom.
19 Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
Kako je mnogo u tebe dobra, koje èuvaš za one koji te se boje, i koje daješ onima koji se u te uzdaju pred sinovima èovjeèijim!
20 Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
Sakrivaš ih pod krov lica svojega od buna ljudskih; sklanjaš ih pod sjen od svadljivijeh jezika.
21 Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
Da je blagosloven Gospod, što mi pokaza divnu milost kao da me uvede u tvrd grad!
22 Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
Ja rekoh u smetnji svojoj: odbaèen sam od oèiju tvojijeh; ali ti èu molitveni glas moj, kad te prizvah.
23 Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
Ljubite Gospoda svi sveti njegovi; Gospod drži vjeru; i uvršeno vraæa onima koji postupaju oholo.
24 Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.
Budite slobodni, i neka bude jako srce vaše, svi koji se u Gospoda uzdate.

< Masalimo 31 >