< Masalimo 30 >

1 Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu. Ndidzakukwezani Yehova, chifukwa mwanditulutsa kwakuya, ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.
For the end, a Psalm and Song at the dedication of the house of David. I will exalt you, O Lord; for you have lifted me up, and not caused mine enemies to rejoice over me.
2 Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo ndipo Inu munandichiritsa.
O Lord my God, I cried to you, and you did heal me.
3 Inu Yehova, munanditulutsa ku manda, munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje. (Sheol h7585)
O Lord, you have brought up my soul from Hades, you have delivered me from [amongst] them that go down to the pit. (Sheol h7585)
4 Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika; tamandani dzina lake loyera.
Sing to the Lord, you his saints, and give thanks for the remembrance of his holiness.
5 Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse; utha kuchezera kulira usiku wonse, koma chimwemwe chimabwera mmawa.
For anger is in his wrath, but life in his favour: weeping shall wait for the evening, but joy shall be in the morning.
6 Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati, “Sindidzagwedezekanso.”
And I said in my prosperity, I shall never be moved.
7 Inu Yehova, pamene munandikomera mtima, munachititsa phiri langa kuyima chilili; koma pamene munabisa nkhope yanu, ndinataya mtima.
O Lord, in your good pleasure you did add strength to my beauty: but you did turn away your face, and I was troubled.
8 Kwa Inu Yehova ndinayitana; kwa Ambuye ndinapempha chifundo;
To you, O Lord, will I cry; and to my God will I make supplication.
9 “Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga ngati nditsikira ku dzenje? Kodi fumbi lidzakutamandani Inu? Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?
What profit is there in my blood, when I go down to destruction? Shall the dust give praise to you? or shall it declare your truth?
10 Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo; Yehova mukhale thandizo langa.”
The Lord heard, and had compassion upon me; the Lord is become my helper.
11 Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina; munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,
You have turned my mourning into joy for me: you have tore off my sackcloth, and girded me with gladness;
12 kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete. Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.
that my glory may sing praise to you, and I may not be pierced [with sorrow]. O Lord my God, I will give thanks to you for ever.

< Masalimo 30 >