< Masalimo 25 >

1 Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
K tebi, Gospode, podižem dušu svoju.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
Bože moj! u tebe se uzdam; ne daj da se osramotim, da mi se ne svete neprijatelji moji.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
I koji se god u te uzdaju, neæe se osramotiti; osramotiæe se oni koji se odmeæu od tebe besputno.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
Pokaži mi, Gospode, putove svoje, nauèi me hoditi stazama tvojim.
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
Uputi me istini svojoj, i nauèi me; jer si ti Bog spasenja mojega, tebi se nadam svaki dan.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
Opomeni se milosrða svojega, Gospode, i milosti svoje; jer su otkako je vijeka.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
Grijehova mladosti moje, i mojih prijestupa ne pominji; po milosti svojoj pomeni mene, radi dobrote svoje, Gospode!
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
Dobar je i pravedan Gospod; toga radi pokazuje grješnicima put.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
Upuæuje krotke istini, uèi krotke hoditi putem njegovijem.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
Svi su putovi Gospodnji milost i istina onima koji drže zavjet njegov i otkrivenje njegovo.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
Radi imena svojega, Gospode, oprosti grijeh moj, jer je velik.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
Koji se èovjek boji Gospoda? On æe mu pokazati koji put da izbere.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
Duša æe njegova u dobru poèivati, i sjeme æe njegovo vladati zemljom.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
Tajna je Gospodnja u onijeh koji ga se boje, i zavjet svoj javlja im.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
Oèi su mi svagda upravljene ka Gospodu, jer on izvlaèi iz zamke noge moje.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
Pogledaj me i smiluj se na me, jer sam inokosan i nevoljnik.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
Nek se raširi stisnuto srce moje, iz tjeskobe moje izvadi me.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
Vidi jade moje i muku moju, i oprosti mi sve grijehe moje.
19 Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
Pogledaj neprijatelje moje kako ih je mnogo i kakvom me pakosnom nenavišæu nenavide.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
Saèuvaj dušu moju i izbavi me; ne daj da se osramotim, jer se u tebe uzdam.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Bezazlenost i pravda neka me saèuva, jer se u tebe uzdam.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!
Izbavi, Bože, Izrailja od svijeh nevolja njegovijeh.

< Masalimo 25 >