< Masalimo 22 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
Bože, Bože moj! zašto si me ostavio udaljivši se od spasenja mojega, od rijeèi vike moje?
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
Bože moj! vièem danju, a ti me ne slušaš, i noæu, ali nemam mira.
3 Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
Sveti, koji živiš u pohvalama Izrailjevim!
4 Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
U tebe se uzdaše oci naši, uzdaše se, i ti si ih izbavljao.
5 Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
Tebe prizivaše, i spasavaše se; u tebe se uzdaše, i ne ostajaše u sramoti.
6 Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
A ja sam crv, a ne èovjek; potsmijeh ljudima i rug narodu.
7 Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
Koji me vide, svi mi se rugaju, razvaljuju usta, mašu glavom,
8 “Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
I govore: oslonio se na Gospoda, neka mu pomože, neka ga izbavi, ako ga miluje.
9 Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
Ta, ti si me izvadio iz utrobe; ti si me umirio na sisi matere moje.
10 Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
Za tobom pristajem od roðenja, od utrobe matere moje ti si Bog moj.
11 Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
Ne udaljuj se od mene; jer je nevolja blizu, a nema pomoænika.
12 Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
Opteèe me mnoštvo telaca; jaki volovi Vasanski opkoliše me;
13 Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
Razvališe na me usta svoja. Lav je gladan lova i rièe.
14 Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
Kao voda razlih se; rasuše se sve kosti moje; srce moje posta kao vosak, rastopilo se u meni.
15 Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
Sasuši se kao crijep krjepost moja, i jezik moj prionu za grlo, i u prah smrtni meæeš me.
16 Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
Opkoliše me psi mnogi; èeta zlikovaca ide oko mene, probodoše ruke moje i noge moje.
17 Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
Mogao bih izbrojiti sve kosti svoje. Oni gledaju, i od mene naèiniše stvar za gledanje.
18 Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
Dijele haljine moje meðu sobom, i za dolamu moju bacaju ždrijeb.
19 Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
Ali ti, Gospode, ne udaljuj se. Silo moja, pohitaj mi u pomoæ.
20 Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
Izbavi od maèa dušu moju, od psa jedinicu moju.
21 Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
Saèuvaj me od usta lavovijeh, i od rogova bivolovih, èuvši, izbavi me.
22 Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
Kazujem ime tvoje braæi; usred skupštine hvaliæu te.
23 Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
Koji se bojite Gospoda, hvalite ga. Sve sjeme Jakovljevo! poštuj ga. Boj ga se, sve sjeme Izrailjevo!
24 Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
Jer se ne ogluši molitve ništega niti je odbi; ne odvrati od njega lica svojega, nego ga usliši kad ga zazva.
25 Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
Tebe æu hvaliti na skupštini velikoj; zavjete svoje svršiæu pred onima koji se njega boje.
26 Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
Neka jedu ubogi i nasite se, i neka hvale Gospoda koji ga traže; živo da bude srce vaše dovijeka.
27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
Opomenuæe se i obratiæe se ka Gospodu svi krajevi zemaljski, i pokloniæe se pred njim sva plemena neznabožaèka.
28 pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
Jer je Gospodnje carstvo; on vlada narodima.
29 Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
Ješæe i pokloniæe se svi pretili na zemlji; pred njim æe pasti svi koji slaze u prah, koji ne mogu saèuvati duše svoje u životu.
30 Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
Sjeme æe njihovo služiti njemu. Kazivaæe se za Gospoda rodu potonjemu.
31 Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.
Doæi æe, i kazivaæe pravdu njegovu ljudima njegovijem, koji æe se roditi; jer je on uèinio ovo.

< Masalimo 22 >