< Masalimo 20 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
Dem Sangmeister. Ein Psalm Davids. Jehovah antworte dir am Tage der Drangsal! Der Name des Gottes Jakobs hebe dich empor!
2 Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
Er sende dir Beistand aus dem Heiligtum, und unterstütze dich aus Zion!
3 Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
Er gedenke aller deiner Speiseopfer, und dein Brandopfer sei fett. (Selah)
4 Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
Er gebe dir nach deinem Herzen, und erfülle alle deine Ratschläge.
5 Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
Lobsingen wollen wir ob Deines Heils, und das Banner erheben im Namen unseres Gottes. Jehovah erfülle dir all deine Bitte.
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
Nun erkenne ich, daß Jehovah Seinen Gesalbten rettet, daß Er ihm antwortet aus den Himmeln Seiner Heiligkeit, durch die Machttaten des Heils Seiner Rechten.
7 Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
Diese gedenken der Streitwagen und jene der Rosse, wir aber des Namens Jehovahs, unseres Gottes.
8 Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
Jene krümmen sich und fallen, wir aber machen uns auf und stehen fest.
9 Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!
Jehovah, rette! Der König antworte uns am Tage, da wir rufen.

< Masalimo 20 >