< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
Nebesa kazuju slavu Božiju, i djela ruku njegovijeh glasi svod nebeski.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
Dan danu dokazuje, i noæ noæi javlja.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
Nema jezika, niti ima govora, gdje se ne bi èuo glas njihov.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
Po svoj zemlji ide kazivanje njihovo i rijeèi njihove na kraj vasiljene. Suncu je postavio stan na njima;
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
I ono izlazi kao ženik iz ložnice svoje, kao junak veselo teèe putem.
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
Izlazak mu je nakraj neba, i hod mu do kraja njegova; i niko nije sakriven od toplote njegove.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
Zakon je Gospodnji svršen, krijepi dušu; svjedoèanstvo je Gospodnje vjerno, daje mudrost nevještome.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
Naredbe su Gospodnje pravedne, vesele srce. Zapovijest je Gospodnja svijetla, prosvjetljuje oèi.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
Strah je Gospodnji èist, ostaje dovijeka. Sudovi su njegovi istini, pravedni svikoliki.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
Bolji su od zlata i dragog kamenja, slaði od meda koji teèe iz sata.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
I slugu tvojega oni su prosvijetlili; ko ih drži ima veliku platu.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Ko æe znati sve svoje pogrješke? Oèisti me i od tajnijeh;
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
I od voljnijeh saèuvaj slugu svojega, da ne obladaju mnome. Tada æu biti svršen i èist od velikoga prijestupa.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
Da su ti rijeèi usta mojih ugodne, i pomisao srca mojega pred tobom, Gospode, krjeposti moja i izbavitelju moj!

< Masalimo 19 >