< Masalimo 19 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
To victorie, the salm of Dauid. Heuenes tellen out the glorie of God; and the firmament tellith the werkis of hise hondis.
2 Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
The dai tellith out to the dai a word; and the nyyt schewith kunnyng to the nyyt.
3 Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
No langagis ben, nether wordis; of whiche the voices of hem ben not herd.
4 Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
The soun of hem yede out in to al erthe; and the wordis of hem `yeden out in to the endis of the world.
5 Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
In the sunne he hath set his tabernacle; and he as a spouse comynge forth of his chaumbre. He fulli ioyede, as a giaunt, to renne his weie;
6 Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
his goynge out was fro hiyeste heuene. And his goyng ayen was to the hiyeste therof; and noon is that hidith hym silf fro his heet.
7 Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
The lawe of the Lord is with out wem, and conuertith soulis; the witnessyng of the Lord is feithful, and yyueth wisdom to litle children.
8 Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
The riytfulnessis of the Lord ben riytful, gladdynge hertis; the comaundement of the Lord is cleere, liytnynge iyen.
9 Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
The hooli drede of the Lord dwellith in to world of world; the domes of the Lord ben trewe, iustified in to hem silf.
10 ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
Desirable more than gold, and a stoon myche preciouse; and swettere than hony and honycoomb.
11 Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
`Forwhi thi seruaunt kepith thoo; myche yeldyng is in tho to be kept.
12 Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
Who vndurstondith trespassis? make thou me cleene fro my priuy synnes;
13 Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
and of alien synnes spare thi seruaunt. `If the forseid defautis ben not, Lord, of me, than Y schal be with out wem; and Y schal be clensid of the mooste synne.
14 Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.
And the spechis of my mouth schulen be, that tho plese; and the thenkynge of myn herte euere in thi siyt. Lord, myn helpere; and myn ayenbiere.

< Masalimo 19 >