< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
For the end, [a Psalm] of David, the servant of the Lord; [the words] which he spoke to the Lord, [even] the words of this Song, in the day in which the Lord delivered him out the hand of all his enemies, and out the hand of Saul: and he said: I will love you, O Lord, my strength.
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
The Lord is my firm support, and my refuge, and my deliverer; my God is my helper, I will hope in him; [he is] my defender, and the horn of my salvation, and my helper.
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
I will call upon the Lord with praises, and I shall be saved from mine enemies.
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
The pangs of death compassed me, and the torrents of ungodliness troubled me exceedingly.
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
The pangs of hell came round about me: the snares of death prevented me. (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
And when I was afflicted I called upon the Lord, and cried to my God: he heard my voice out of this holy temple, and my cry shall enter before him, [even] into his ears.
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
Then the earth shook and quaked, and the foundations of the mountains were disturbed, and were shaken, because God was angry with them.
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
There went up a smoke in his wrath, and fire burst into a flame at his presence: coals were kindled at it.
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
And he bowed the heaven, and came down: and thick darkness was under his feet.
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
And he mounted on cherubs and flew: he flew on the wings of winds.
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
And he made darkness his secret place: round about him was his tabernacle, [even] dark water in the clouds of the air.
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
At the brightness before him the clouds passed, hail and coals of fire.
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
The Lord also thundered from heaven, and the Highest uttered his voice.
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
And he sent forth [his] weapons, and scattered them; and multiplied lightnings, and routed them.
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
And the springs of waters appeared, and the foundations of the world were exposed, at your rebuke, O Lord, at the blasting of the breath of your wrath.
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
He sent from on high and took me, he drew me to himself out of many waters.
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
He will deliver me from my mighty enemies, and from them that hate me; for they are stronger than I.
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
They prevented me in the day of mine affliction: but the Lord was my stay against [them].
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
And he brought me out into a wide place: he will deliver me, because he has pleasure in me.
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
And the Lord will recompense me according to my righteousness; even according to the purity of my hands will he recompense me.
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
For I have kept the way of the Lord and have not wickedly departed from my God.
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
For all his judgements were before me, and his ordinances departed not from me.
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
And I shall be blameless with hem, and shall keep myself from mine iniquity.
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
And the Lord shall recompense me according to my righteousness, and according to the purity of my hands before his eyes.
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
With the holy you will be holy; and with the innocent man you will be innocent.
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
And with the excellent [man] you will be excellent; and with the perverse you will show frowardness.
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
For you will save the lowly people, and will humble the eyes of the proud.
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
For you, O Lord, will light my lamp: my God, you will lighten my darkness.
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
For by you shall I be delivered from a troop; and by my God I will pass over a wall.
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
[As for] my God, his way is perfect: the oracles of the Lord are tried in the fire; he is a protector of all them that hope in him.
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
For who is God but the Lord? and who is a God except our God?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
[It is] God that girds me with strength, and has made my way blameless:
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
who strengthens my feet as hart's feet, and sets me upon high places.
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
He instructs my hands for war: and you have made my arms [as] a brazen bow.
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
And you have made me secure in my salvation: and your right hand has helped me, and your correction has upheld me to the end; yes, your correction itself shall instruct me.
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
You has made room for my goings under me, and by footsteps did not fail.
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
I will pursue mine enemies, and overtake them; and I will not turn back until they are consumed.
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
I will dash them to pieces and they shall not be able to stand: they shall fall under my feet.
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
For you have girded me with strength for war: you have beaten down under me all that rose up against me.
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
And you has made mine enemies turn their backs before me; and you have destroyed them that hated me.
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
They cried, but there was no deliverer: [even] to the Lord, but he listened not to them.
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
I will grind them as the mud of the streets: and I will beat them small as dust before the wind.
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
Deliver me from the gain sayings of the people: you shall make me head of the Gentiles: a people whom I knew not served me,
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
at the hearing of the ear they obeyed me: the strange children lied to me.
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
The strange children waxed old, and fell away from their paths through lameness.
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
The Lord lives; and blessed [be] my God; and let the God of my salvation be exalted.
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
[It is] God that avenges me, and has subdued the nations under me;
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
my deliverer from angry enemies: you shall set me on high above them that rise up against me: you shall deliver me from the unrighteous man.
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
Therefore will I confess to you, O Lord, amongst the Gentiles, and sing to your name.
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
[God] magnifies the deliverances of his king; and deals mercifully with David his anointed, and his seed, for ever.

< Masalimo 18 >