< Masalimo 18 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
耶和華的僕人大衛的詩,交與伶長。當耶和華救他脫離一切仇敵和掃羅之手的日子,他向耶和華念這詩的話。說: 耶和華,我的力量啊,我愛你!
2 Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
耶和華是我的巖石,我的山寨,我的救主, 我的上帝,我的磐石,我所投靠的。 他是我的盾牌, 是拯救我的角,是我的高臺。
3 Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
我要求告當讚美的耶和華; 這樣我必從仇敵手中被救出來。
4 Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
曾有死亡的繩索纏繞我, 匪類的急流使我驚懼,
5 Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
陰間的繩索纏繞我, 死亡的網羅臨到我。 (Sheol h7585)
6 Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
我在急難中求告耶和華, 向我的上帝呼求。 他從殿中聽了我的聲音; 我在他面前的呼求入了他的耳中。
7 Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
那時,因他發怒,地就搖撼戰抖; 山的根基也震動搖撼。
8 Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
從他鼻孔冒煙上騰; 從他口中發火焚燒,連炭也着了。
9 Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
他又使天下垂,親自降臨, 有黑雲在他腳下。
10 Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
他坐着基路伯飛行; 他藉着風的翅膀快飛。
11 Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
他以黑暗為藏身之處, 以水的黑暗、天空的厚雲為他四圍的行宮。
12 Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
因他面前的光輝, 他的厚雲行過便有冰雹火炭。
13 Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
耶和華也在天上打雷; 至高者發出聲音便有冰雹火炭。
14 Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
他射出箭來,使仇敵四散; 多多發出閃電,使他們擾亂。
15 Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
耶和華啊,你的斥責一發, 你鼻孔的氣一出, 海底就出現, 大地的根基也顯露。
16 Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
他從高天伸手抓住我, 把我從大水中拉上來。
17 Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
他救我脫離我的勁敵和那些恨我的人, 因為他們比我強盛。
18 Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
我遭遇災難的日子,他們來攻擊我; 但耶和華是我的倚靠。
19 Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
他又領我到寬闊之處; 他救拔我,因他喜悅我。
20 Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
耶和華按着我的公義報答我, 按着我手中的清潔賞賜我。
21 Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
因為我遵守了耶和華的道, 未曾作惡離開我的上帝。
22 Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
他的一切典章常在我面前; 他的律例我也未曾丟棄。
23 Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
我在他面前作了完全人; 我也保守自己遠離我的罪孽。
24 Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
所以,耶和華按我的公義, 按我在他眼前手中的清潔償還我。
25 Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
慈愛的人,你以慈愛待他; 完全的人,你以完全待他。
26 kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
清潔的人,你以清潔待他; 乖僻的人,你以彎曲待他。
27 Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
困苦的百姓,你必拯救; 高傲的眼目,你必使他降卑。
28 Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
你必點着我的燈; 耶和華-我的上帝必照明我的黑暗。
29 Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
我藉着你衝入敵軍, 藉着我的上帝跳過牆垣。
30 Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
至於上帝,他的道是完全的; 耶和華的話是煉淨的。 凡投靠他的,他便作他們的盾牌。
31 Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
除了耶和華,誰是上帝呢? 除了我們的上帝,誰是磐石呢?
32 Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
惟有那以力量束我的腰、 使我行為完全的,他是上帝。
33 Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
他使我的腳快如母鹿的蹄, 又使我在高處安穩。
34 Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
他教導我的手能以爭戰, 甚至我的膀臂能開銅弓。
35 Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
你把你的救恩給我作盾牌; 你的右手扶持我; 你的溫和使我為大。
36 Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
你使我腳下的地步寬闊; 我的腳未曾滑跌。
37 Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
我要追趕我的仇敵,並要追上他們; 不將他們滅絕,我總不歸回。
38 Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
我要打傷他們,使他們不能起來; 他們必倒在我的腳下。
39 Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
因為你曾以力量束我的腰,使我能爭戰; 你也使那起來攻擊我的都服在我以下。
40 Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
你又使我的仇敵在我面前轉背逃跑, 叫我能以剪除那恨我的人。
41 Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
他們呼求,卻無人拯救; 就是呼求耶和華,他也不應允。
42 Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
我搗碎他們,如同風前的灰塵, 倒出他們,如同街上的泥土。
43 Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
你救我脫離百姓的爭競, 立我作列國的元首; 我素不認識的民必事奉我。
44 Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
他們一聽見我的名聲就必順從我; 外邦人要投降我。
45 Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
外邦人要衰殘, 戰戰兢兢地出他們的營寨。
46 Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
耶和華是活神。 願我的磐石被人稱頌; 願救我的上帝被人尊崇。
47 Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
這位上帝,就是那為我伸冤、 使眾民服在我以下的。
48 amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
你救我脫離仇敵, 又把我舉起,高過那些起來攻擊我的; 你救我脫離強暴的人。
49 Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
耶和華啊,因此我要在外邦中稱謝你, 歌頌你的名。
50 Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.
耶和華賜極大的救恩給他所立的王, 施慈愛給他的受膏者, 就是給大衛和他的後裔,直到永遠。

< Masalimo 18 >