< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
For the end, a Psalm of David. O Lord, you have proved me, and known me.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
You know my down-sitting and mine up-rising: you understand my thoughts long before.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
You have traced my path and my bed, and have foreseen all my ways.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
For there is no unrighteous word in my tongue: behold, O Lord, you have known all things,
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
the last and the first: you have fashioned me, and laid your hand upon me.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
The knowledge of you is too wonderful for me; it is very difficult, I can’t [attain] to it.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Whither shall I go from your Spirit? and whither shall I flee from my presence?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
If I should go up to heaven, you are there: if I should go down to hell, you are present. (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
If I should spread my wings [to fly] straight forward, and sojourn at the extremity of the sea, [it would be vain],
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
for even there your hand would guide me, and your right hand would hold me.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
When I said, Surely the darkness will cover me; even the night [was] light in my luxury.
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
For darkness will not be darkness with you; but night will be light as day: as its darkness, so shall its light [be to you].
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
For you, O Lord, have possessed my reins; you have helped me from my mother's womb.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
I will give you thanks; for you are fearfully wondrous; wondrous are your works; and my soul knows [it] well.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
My bones, which you made in secret were not hidden from you, nor my substance, in the lowest parts of the earth.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Your eyes saw my unwrought [substance], and all [men] shall be written in your book; they shall be formed by day, though [there should for a time] be no one amongst them.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
But your friends, O God, have been greatly honoured by me; their rule has been greatly strengthened.
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
I will number them, and they shall be multiplied beyond the sand; I awake, and am still with you.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Oh that you would kill the wicked, O God; depart from me, you men of blood.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
For you will say concerning [their] thought, [that] they shall take your cities in vain.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Have I not hated them, O Lord, that hate you? and wasted away because of your enemies?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
I have hated them with perfect hatred; they were counted my enemies.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Prove me, O God, and know my heart; examine me, and know my paths;
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
and see if [there is any] way of iniquity in me, and lead me in an everlasting way.

< Masalimo 139 >