< Masalimo 121 >

1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
A Song of Degrees. I lifted up mine eyes to the mountains, whence my help shall come.
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
My help [shall come] from the Lord, who made the heaven and the earth.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Let not your foot be moved; and let not your keeper slumber.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Behold, he that keeps Israel shall not slumber nor sleep.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
The Lord shall keep you: the Lord is your shelter upon your right hand.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
The sun shall not burn you by day, neither the moon by night.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
May the Lord preserve you from all evil: the Lord shall keep your soul.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
The Lord shall keep your coming in, and your going out, from henceforth and even for ever.

< Masalimo 121 >