< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
in finem pro octava psalmus David salvum me fac Domine quoniam defecit sanctus quoniam deminutae sunt veritates a filiis hominum
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
vana locuti sunt unusquisque ad proximum suum labia dolosa in corde et corde locuti sunt
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
disperdat Dominus universa labia dolosa linguam magniloquam
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
qui dixerunt linguam nostram magnificabimus labia nostra a nobis sunt quis noster dominus est
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
propter miseriam inopum et gemitum pauperum nunc exsurgam dicit Dominus ponam in salutari fiducialiter agam in eo
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
eloquia Domini eloquia casta argentum igne examinatum probatum terrae purgatum septuplum
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
tu Domine servabis nos et custodies nos a generatione hac et in aeternum
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
in circuitu impii ambulant secundum altitudinem tuam multiplicasti filios hominum

< Masalimo 12 >