< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Alef. Blagor poštenim na potu, kateri hodijo po postavi Gospodovi.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blagor njim, ki hranijo pričanja njegova, ki ga iščejo iz vsega srca.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Kateri tudi ne delajo krivice, ampak hodijo po potih njegovih.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Ti si zapovedal ukaze svoje, da naj se spolnjujejo pridno.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O da bi bila pota moja obernena spolnjevat postave tvoje!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Tedaj se ne osramotim, ko bodem gledal vse zapovedi tvoje.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Slavil te bodem s pravim srcem; učil se sodbâ pravice tvoje.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Postave tvoje bodem spolnjeval, ne zapusti me tako!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Bet. Kako bode deček čistil stezo svojo? Držeč se je poleg besede tvoje.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Iz vsega srca svojega te iščem, ne daj, da izgrešim zapovedi tvoje.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
V srci svojem hranim govor tvoj, da ne grešim zoper tebe.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Ti blagoslavljeni Gospod, uči me postave svoje.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Z ustnami svojimi preštevam vse pravice tvojih ust,
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Veselim se pota pričanj tvojih, kakor vseh zakladov.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Zapovedi tvoje premišljujem in gledam steze tvoje.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
V postavah tvojih se razveseljujem, besede tvoje ne zabim.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Gimel. Dobroto podéli hlapcu svojemu, dokler živim spolnjujem naj besedo tvojo.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Odgrni oči moje, da gledam čuda po zakonu tvojem.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Tujec sem na tej zemlji, ne skrivaj mi zapovedi svojih.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Ginem od hrepenenja po pravicah tvojih vsak čas.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Ti pogubljaš prevzetne, proklete, kateri izgrešajo zapovedi tvoje.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Odvali od mene sramoto in zaničevanje, ker hranim pričanja tvoja.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Tedaj prvaki sedé in govoré zoper mene, hlapec tvoj premišlja postave tvoje.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Tedaj so pričanja tvoja razveseljevanja moja, svetovalci moji.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Dalet. V prahu tiči življenje moje, živega me ohrani po besedi svoji.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Pota svoja sem prešteval, in ti si me uslišal; úči me postave svoje.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Daj, da umem pot zapovedi tvojih, da premišljam čuda tvoja.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Od otožnosti solzi duša moja, dvigni me po besedi svoji.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Krivičnosti pot odvrni od mene, in zakon svoj mi podéli milostno.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Resnice pot volim, sodbe tvoje imam pred očmi.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Držim se pričanj tvojih, Gospod; ne daj, da se osramotim.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Po potih zapovedi tvojih bodem tekal, ko bodeš razširil srce moje.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
He. Uči me, Gospod, postav tvojih pót, katero bodem hranil do konca.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Daj, da umem, da hranim zakon tvoj, in da ga spolnjujem iz vsega srca.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Daj, da hodim po zapovedi tvojih poti, ker tá me razveseljuje.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Nagni srce moje k postavam svojim, in ne k dobičku.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Odvrni oči moje, da ne gledajo ničemurnosti; po potih tvojih daj da živim.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Stóri govor svoj hlapcu svojemu, kateri je vdan strahu pred teboj.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Odvrni sramoto mojo, katere se bojim, ker dobre so pravice tvoje.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Glej, ukazov tvojih želim, v pravici tvoji daj mi živeti.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Vav. Ko mi bodejo prišle milosti tvoje, Gospod; blaginja tvoja po govoru tvojem,
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Odgovoril bodem njemu, ki me sramoti, kakor je; ker zaupanje imam v besedo tvojo.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Ali od ust mojih ne odvzemi besede svoje resnične; ker pravic tvojih čakam.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
In spolnjeval bodem zakon tvoj vedno, vekomaj in vekomaj.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
In neprestano bodem hodil po sami širjavi, ker povelj tvojih iščem.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
In govoril bodem o pričanjih tvojih pred kralji, in ne bode me sram.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
In razveseljujoč se v zapovedih tvojih, katere ljubim,
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Dvignil bodem roke svoje do povelj tvojih, katera ljubim, in premišljeval postave tvoje.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Zajin. Spomni se besede svoje s hlapcem svojim, o kateri si mi dal upanje.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
To je tolažilo moje v bridkosti moji; da me govor tvoj oživlja.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Prevzetniki se mi posmehujejo silno, od postave tvoje ne zavijem.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Spominjam so sodbà tvojih od vekomaj, Gospod, in samega sebe tolažim.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Vihar me grabi od krivičnih, ki zapuščajo zakon tvoj.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Prepevanju predmet so mi postave tvoje v kraji popotovanj mojih.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Ponoči se spominjam imena tvojega, Gospod; in zakon tvoj spolnjujem.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
To je tolažba meni, da hranim zapovedi tvoje.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Het. Delež moj si, Gospod, pravim, da spolnjujem besede tvoje.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Obličje tvoje molim iz vsega srca svojega; milost mi izkaži po govoru svojem.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Pota svoja premišljam, da obračam noge svoje po pričanjih tvojih.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Hitim in se ne mudim spolnjevat zapovedi tvoje.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Krdela krivičnih me plenijo, a postave tvoje ne zabim.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
O polunoči vstajam slavit te, zavoljo zapovedi tvojih pravičnih.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Tovariš sem vsem, kateri te česté in spolnjujejo povelja tvoja.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Milosti tvoje, o Gospod, polna je zemlja; postave svoje me úči.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tet. Dobro si storil hlapcu svojemu, Gospod; po besedi svoji.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Izvrstnost pameti in vednosti me úči; ker zapovedim tvojim verujem.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Ko nisem še govoril, motil sem se; sedaj pa spolnjujem govor tvoj.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Dober si in dobrotljiv, úči me postave svoje.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Ko zvijačo napravljajo zoper mene prevzetniki, jaz iz vsega srca hranim povelja tvoja.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Debelí se kakor z mastjo njih srce; jaz se zakona tvojega radujem.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Na dobro mi je bila bridkost, da bi se učil postav tvojih.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Boljši mi je zakon tvojih ust nego mnogo tisoč zlatnikov in srebernikov.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Jod. Roke tvoje so me naredile in napravile me; storí me razumnega, da se učim povelj tvojih.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Boječi se tebe naj me vidijo ter se veselé, ker imam v besedi tvoji nado svojo.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Spoznavam, Gospod, da so pravične sodbe tvoje; in da si me v zvestobi ponižal.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Pridi skoraj milost tvoja, da me tolaži, po govoru tvojem s tvojim hlapcem.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Dojdejo naj mi usmiljenja tvoja, da živim; ker zakon je vse razveseljevanje moje.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Osramoté se naj prevzetniki, ker mi hudo delajo po krivem, ko premišljujem povelja tvoja.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Povrnejo se naj k meni boječi se tebe in poznajoči pričanja tvoja.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Srce moje bode pošteno v postavah tvojih, da se ne osramotim.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Kaf. Duša moja koperni po blaginji tvoji; v besedi tvoji imam nado.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Oči moje koperné po govoru tvojem, ko govorim: Kedaj me bodeš potolažil?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Dasì sem podoben mehu v dimu, postav tvojih nisem pozabil.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Koliko bode dnî hlapca tvojega? Kedaj bodeš sodil nje, ki me preganjajo?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Jame mi kopljejo prevzetniki, kateri se ne ravnajo po zakonu tvojem.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Vsa povelja tvoja zgolj resnica; po krivem me preganjajo, pomagaj mi.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Skoraj so me uničili vrženega na tla; jaz pa se nísem izneveril postavam tvojim.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Po milosti svoji ohrani me živega, da spolnjujem pričanja tvojih ust.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Lamed. Vekomaj, o Gospod, biva beseda tvoja v nebesih,
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Od roda do roda zvestoba tvoja; ko si ustanavljal zemljo, stala je ona.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Po sodbah tvojih stoji vse še danes; ker vse ono služi tebi.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Ako bi ne bil zakon tvoj vse razveseljevanje moje, zdavnaj že bi bil poginil v nadlogi svoji.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Vekomaj ne pozabim povelj tvojih, ker z njimi hraniš me živega.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Tvoj sem, hrani me, ker povelj tvojih iščem.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Ko me čakajo krivični, da me pogubé, pregledujem pričanja tvoja.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Sleherne popolnosti vidim da je konec; povelje tvoje pa je obširno silno.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Mem. Kako ljubim zakon tvoj! ves dan je premišljevanje moje.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Modrejšega od sovražnikov mojih me dela po poveljih tvojih; ker vekomaj mi je na strani.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Razumnejši postajam od vseh učenikov svojih; ker pričanja tvoja so premišljevanje moje.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Razumnejši sem od starcev, ker hranim povelja tvoja.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Od vsake hudobne steze zadržujem noge svoje, da spolnjujem besedo tvojo.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Od sodbâ tvojih se ne ganem, ker ti me učiš.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Kako sladki so mojemu grlu govori tvoji! sladkejši od medú ustom mojim.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Po poveljih tvojih sem razumen, zatorej sovražim vsako stezo krivičnosti.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Nun. Svetilo nogi moji je beseda tvoja, in poti moji luč.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Prisegel sem, kar bodem držal, da bodem spolnjeval pravične sodbe tvoje.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Ponižan sem silno, Gospod; živega me ohrani, po besedi svoji.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Prostovoljne daritve ust mojih sprejemaj, prosim, Gospod; in pravice svoje me úči.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Duša moja je vedno v roki moji; vendar ne zabim tvojega zakona.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Mogočni krivičniki mi stavijo zanko, vendar od povelj tvojih ne zajdem.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Pričanja tvoja imam vekomaj, ker so veselje mojemu srcu.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Srce svoje nagibljem, da spolnjuje postave tvoje, vekomaj, večno!
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Sameh. Misli druge sovražim, zakon pa tvoj ljubim.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Zatišje si moje in ščit moj; v besedi tvoji imam nado.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Umaknite se od mene, hudobni, da hranim ukaze svojega Boga.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Podpiraj me po govoru svojem, da živim; in ne osramoti me v nadi moji.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Podpiraj me, da bodem otét, in da gledam vedno na postave tvoje.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Vse, kateri izgrešujejo postave tvoje, teptaš; ker krivična je njih zvijača.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Kakor žlindro odpravljaš vse krivične sè zemlje; zatorej ljubim pričanja tvoja.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Od strahú pred teboj trepeče meso moje; tako me je strah tvojih sodbâ.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Hajin. Po sodbi delam in pravici; ne izročaj me njim, ki me stiskajo.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Porok bodi hlapcu svojemu na dobro; da me ne zatirajo prevzetni.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Oči moje koperné po blaginji tvoji, in po pravičnem govoru tvojem.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Ravnaj po milosti svoji s hlapcem svojim; in postave svoje me úči.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Hlapec sem tvoj, storí me razumnega, da spoznam pričanja tvoja.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Čas je, da dela Gospod; v nič dévajo zakon tvoj.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Zatorej bolj ljubim ukaze tvoje, ko zlato in sicer najčistejše.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Zato spoznavam vse ukaze za prave; vsako stezo krivičnosti sovražim.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Pe. Čudovita so pričanja tvoja; zatorej jih hrani duša moja.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Dohod besed tvojih razsvetljuje; z razumnostjo podučuje preproste.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Usta svoja raztezam in sopiham; ker želján sem ukazov tvojih.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Ozri se v mé in storí mi milost; kakor je prav proti njim, kateri ljubijo ime tvoje.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Noge moje utrdi v govoru svojem, in ne daj da gospoduje kaka krivica z menoj.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Otmi me zatiranja ljudî, da spolnjujem postave tvoje.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Daj, da sveti tvoje obličje pred hlapcem tvojim; in úči me postave svoje.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Potoki vodâ tekó iz mojih oči, zaradi njih, ki ne spolnjujejo tvojega zakona.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Sade. Pravičen si, Gospod, in raven v sodbah svojih.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Ukazal si pravična pričanja svoja, in silno zvesta.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Od gorečnosti svoje ginem, ker besede tvoje zabijo sovražniki moji.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Čist je govor tvoj močno; zatorej ga ljubi hlapec tvoj.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Majhen sem jaz in zaničevan; povelj tvojih ne zabim,
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Pravice tvoje, vedne pravice, in postave tvoje resnične.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Zatiranje in stiska me obhajati; ukazi tvoji so razveseljevanje moje.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Pravica pričanj tvojih je vekomaj; razumnega me naredi, da živim.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Kof. Ko te kličem iz vsega srca, usliši me, Gospod, da hranim postave tvoje.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Ko te kličem, reši me, da spolnjujem pričanja tvoja.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Préd te pridem v somraku, da vpijem; v besedo tvojo imam upanje.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Oči moje prehitujejo straže, premišljat govor tvoj.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Glas moj poslušaj po milosti svoji, Gospod; po sodbah svojih ohrani me živega,
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ko se bližajo pregrehe učenci, ki so daleč od zakona tvojega,
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Blizu si, Gospod; in vsi ukazi tvoji so resnica.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Zdavnaj vem o pričanjih tvojih, da si jih ustanovil vekomaj.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Reš. Ozri se v nadlogo mojo, in reši me; ker zakona tvojega ne zabim.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Prevzemi pravdo mojo in reši me; po govoru svojem ohrani me živega.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Daleč od krivičnih bodi blaginja, ker ne iščejo postav tvojih.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Usmiljenje tvoje je obilo, Gospod; po sodbah tvojih, ohrani me živega.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Dasì je mnogo preganjalcev mojih in sovražnikov mojih, od pričanj tvojih ne krenem.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Kakor hitro vidim izdajalce, mučim z gnjusom samega sebe, ker se ne držé govora tvojega.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Glej, da ljubim povelja tvoja, Gospod; po milosti svoji ohrani me živega.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Preblaga beseda tvoja je sama resnica; in vekomaj je vsaka pravična sodba tvoja.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Šin. Ko me preganjajo po nedolžnem prvaki; boji se besede tvoje moje srce.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Veselim se govora tvojega; kakor kdor je našel plen obilen.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Krivičnost sovražim in studim, zakon tvoj ljubim.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sedemkrat te hvalim na dán za pravične sodbe tvoje.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Velik mir imajo, kateri ljubijo zakon tvoj, in ní jim izpotike.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Blaginje tvoje čakam, Gospod; in ukaze tvoje spolnjujem.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Duša moja spolnjuje pričanja tvoja, in ljubim jih močno.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Povelja tvoja spolnjujem in pričanja tvoja, ker vsa pota moja so pred teboj.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Tav. Vpitje moje se bližaj tvojemu obličju, Gospod; po besedi svoji naredi me umnega.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Molitev moja pridi pred obličje tvoje; po govoru svojem otmi me.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Hvala bodo vrela z ustnic mojih, ko me bodeš učil postave svoje.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Jezik moj bode prepeval govor tvoj, da so prepravične vse zapovedi tvoje.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
V pomoč mi bodi na strani roka tvoja; ker volim povelja tvoja.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Po blaginji tvoji hrepenim, Gospod; in zakon tvoj je vse razveseljevanje moje.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Živi duša moja, da hvali tebe; in sodbe tvoje naj pomagajo meni.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Potikam se kakor ovca izgubljena, išči svojega hlapca; ker povelj tvojih ne zabim.

< Masalimo 119 >