< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Alef Błogosławieni ci, których droga jest nieskalana, którzy zgodnie z prawem PANA postępują.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Błogosławieni ci, którzy strzegą jego świadectw i szukają go całym sercem;
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
[Którzy] nie czynią nieprawości, [ale] chodzą jego drogami.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Ty rozkazałeś pilnie przestrzegać twoich nakazów.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oby moje drogi były skierowane na przestrzeganie twoich praw!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Wtedy nie doznam wstydu, gdy będę zważał na wszystkie twoje przykazania.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Będę cię wysławiał w szczerości serca, gdy nauczę się twoich sprawiedliwych praw.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Będę przestrzegał twoich praw, nigdy mnie nie opuszczaj.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Bet W jaki sposób oczyści młodzieniec swoją ścieżkę? Gdy zachowuje się według twego słowa.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Z całego serca cię szukam, nie pozwól mi zboczyć od twoich przykazań.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
W swoim sercu zachowuję twoje słowa, aby nie zgrzeszyć przeciwko tobie.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Błogosławiony jesteś, PANIE; naucz mnie twoich praw.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Swoimi wargami opowiadam wszystkie nakazy twoich ust.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Cieszę się drogą twoich świadectw bardziej niż z wszelkiego bogactwa.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Rozmyślam o twoich przykazaniach i przypatruję się twoim drogom.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Rozkoszuję się twoimi prawami i nie zapominam twoich słów.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Gimel Okaż dobroć swemu słudze, [abym] żył i przestrzegał twoich słów.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Otwórz moje oczy, abym ujrzał cuda twego prawa.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Jestem obcym na ziemi, nie ukrywaj przede mną twoich przykazań.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Moja dusza omdlewa, tęskniąc cały czas za twoimi sądami.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Zgromiłeś pysznych, przeklęci [są ci], którzy odstępują od twoich przykazań.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Oddal ode mnie hańbę i wzgardę, gdyż przestrzegam twoich świadectw.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Władcy też zasiadają i mówią przeciwko mnie, lecz twój sługa rozmyśla o twoich prawach.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Twoje świadectwa też są moją rozkoszą [i] moimi doradcami.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Dalet Moja dusza przylgnęła do prochu, ożyw mnie według twego słowa.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Opowiedziałem [ci] moje drogi i wysłuchałeś mnie; naucz mnie twoich praw.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Spraw, bym zrozumiał drogę twoich nakazów, a będę rozmyślał o twoich cudownych dziełach.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Dusza moja rozpływa się [we łzach] ze smutku, umocnij mnie według twego słowa.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Oddal ode mnie drogę kłamstwa, a obdarz mnie swoim prawem.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Wybrałem drogę prawdy, a twoje nakazy stawiam [przed sobą].
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Przylgnąłem do twoich świadectw; PANIE, nie pozwól mi zaznać wstydu.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Pobiegnę drogą twoich przykazań, gdy rozszerzysz moje serce.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
He Naucz mnie, PANIE, drogi twoich praw, a będę jej strzegł [aż] do końca.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Daj mi rozum, abym zachował twoje prawo; żebym go przestrzegał z całego serca.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Spraw, bym chodził ścieżką twoich przykazań, gdyż w nich mam upodobanie.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Nakłoń moje serce do twoich świadectw, a nie do chciwości.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Odwróć moje oczy, aby nie patrzyły na marność, ożyw mnie na twojej drodze.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Utwierdź swoje słowo względem twego sługi, który się oddał twojej bojaźni.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Oddal ode mnie mą hańbę, której się boję, bo twoje sądy [są] dobre.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Oto pragnę twoich nakazów; ożyw mnie w swej sprawiedliwości.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Waw Niech zstąpi na mnie twoja łaskawość, PANIE, twoje zbawienie według twego słowa;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Abym mógł dać odpowiedź temu, który mi urąga, bo ufam twojemu słowu.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
I nie wyjmuj z moich ust słowa prawdy, bo twoich sądów oczekuję.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
I będę zawsze strzegł twego prawa, na wieki wieków.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
A będę chodził drogą przestronną, bo szukam twoich nakazów.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Owszem, będę mówił o twoich świadectwach przed królami i nie doznam wstydu.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Będę się rozkoszował twoimi przykazaniami, które umiłowałem.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Wznoszę też swoje ręce ku twoim przykazaniom, które miłuję, i będę rozmyślał o twoich prawach.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Zain Pamiętaj o słowie danym twemu słudze, na którym [to słowie] kazałeś mi polegać.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
To jest moja pociecha w utrapieniu, bo twoje słowo mnie ożywia.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Pyszni bardzo się ze mnie naśmiewają, lecz nie odstępuję od twego prawa.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Pamiętam o twoich wiecznych sądach, PANIE, i pocieszam się nimi.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Strach mnie ogarnął z powodu niegodziwych, którzy porzucają twoje prawo.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Twoje prawa są dla mnie pieśniami w domu mego pielgrzymowania.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Nocą wspominam twoje imię, PANIE, i strzegę twego prawa.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
To mam, bo przestrzegam twoich przykazań.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Het PANIE, [ty jesteś] moim udziałem, przyrzekłem przestrzegać twoich słów.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Modliłem się przed twoim obliczem z całego serca, zlituj się nade mną według twego słowa.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Rozmyślałem nad moimi drogami i zwracałem kroki ku twoim świadectwom.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Spieszyłem się i nie zwlekałem z przestrzeganiem twoich przykazań.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Hufce niegodziwych złupiły mnie, [ale] nie zapominam twojego prawa.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
O północy wstaję, aby wysławiać cię za twoje sprawiedliwe sądy.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Jestem przyjacielem wszystkich, którzy boją się ciebie, i tych, którzy przestrzegają twoich przykazań.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
PANIE, ziemia jest pełna twego miłosierdzia; naucz mnie twoich praw.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tet Wyświadczyłeś dobro twemu słudze, PANIE, według twego słowa.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Naucz mnie trafnego sądu i wiedzy, bo uwierzyłem twoim przykazaniom.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Zanim doznałem utrapienia, błądziłem; lecz teraz przestrzegam twego słowa.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Jesteś dobry i czynisz dobro; naucz mnie twoich praw.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Zuchwali zmyślili przeciwko mnie kłamstwo, [ale] ja całym sercem strzegę twoich przykazań.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Serce ich utyło jak sadło, [ale] ja rozkoszuję się twoim prawem.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Dobrze to dla mnie, że zostałem uciśniony, abym się nauczył twoich praw.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Prawo twoich ust [jest] lepsze dla mnie niż tysiące [sztuk] złota i srebra.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Jod Twoje ręce mnie uczyniły i ukształtowały; daj mi rozum, abym się nauczył twoich przykazań;
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Bojący się ciebie, widząc mnie, będą się radować, że pokładam nadzieję w twoim słowie.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Wiem, PANIE, że twoje sądy [są] sprawiedliwe i [że] słusznie mnie trapiłeś.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Proszę cię, niech mnie ucieszy twoje miłosierdzie według twego słowa do twego sługi.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Niech przyjdzie na mnie twoje miłosierdzie, abym żył; bo twoje prawo jest moją rozkoszą.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Niech się zawstydzą zuchwali, bo niesłusznie znieważali mnie, ale ja będę rozmyślać o twoich przykazaniach.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Niech się zwrócą do mnie ci, którzy się boją ciebie, i ci, którzy znają twoje świadectwa.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Niech moje serce będzie nienaganne w twoich prawach, abym nie doznał wstydu.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Kaf Moja dusza tęskni do twego zbawienia, pokładam nadzieję w twoim słowie.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Moje oczy słabną, [czekając] na twoje słowo, gdy mówię: Kiedy mnie pocieszysz?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Chociaż jestem jak bukłak w dymie, [jednak] nie zapomniałem twoich praw.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Ile będzie dni twego sługi? Kiedy wykonasz wyrok na tych, którzy mnie prześladują?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Doły wykopali dla mnie zuchwali, którzy nie postępują według twego prawa.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Wszystkie twoje przykazania są prawdą; bez powodu mnie prześladują; pomóż mi.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Omal nie zgładzili mnie na ziemi; ja zaś nie porzuciłem twoich przykazań.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Według twego miłosierdzia ożyw mnie, abym strzegł świadectwa twoich ust.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Lamed Na wieki, o PANIE, twoje słowo trwa w niebie.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Z pokolenia na pokolenie twoja prawda; ugruntowałeś ziemię i trwa.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
[Wszystko] trwa do dziś według twego rozporządzenia; to wszystko służy tobie.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Gdyby twoje prawo nie było moją rozkoszą, dawno zginąłbym w moim utrapieniu.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nigdy nie zapomnę twoich przykazań, bo nimi mnie ożywiłeś.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Twoim jestem, wybaw mnie, bo szukam twoich przykazań.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Czyhają na mnie niegodziwi, aby mnie stracić, [ale ja] rozważam twoje świadectwa.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Widziałem koniec wszelkiej doskonałości, [ale] twoje przykazanie jest bezkresne.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Mem O, jakże miłuję twoje prawo! Przez cały dzień o nim rozmyślam.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Czynisz mnie mądrzejszym od moich nieprzyjaciół dzięki twoim przykazaniom, bo mam je zawsze przed sobą.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Stałem się rozumniejszy od wszystkich moich nauczycieli, bo rozmyślam o twoich świadectwach.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Jestem roztropniejszy od starszych, bo przestrzegam twoich przykazań.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Powstrzymuję swoje nogi od wszelkiej drogi złej, abym strzegł twego słowa.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Nie odstępuję od twoich nakazów, bo ty mnie uczysz.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
O, jakże słodkie są twoje słowa dla mego podniebienia! [Są słodsze] niż miód dla moich ust.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Dzięki twoim przykazaniom nabywam rozumu; dlatego nienawidzę wszelkiej ścieżki fałszywej.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Nun Twoje słowo jest pochodnią dla moich nóg i światłością na mojej ścieżce.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Złożyłem przysięgę i wypełnię ją, będę przestrzegał twoich sprawiedliwych nakazów.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Jestem bardzo strapiony; PANIE, ożyw mnie według słowa twego.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
PANIE, przyjmij dobrowolne ofiary moich ust i naucz mnie twoich nakazów.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Moja dusza jest stale w niebezpieczeństwie, ale nie zapominam twojego prawa.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Niegodziwi zastawili na mnie sidła, lecz [ja] nie odstępuję od twoich przykazań.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Wziąłem twoje świadectwa jako wieczne dziedzictwo, bo są radością mego serca.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Nakłoniłem moje serce, by zawsze wykonywać twoje prawa, aż do końca.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Samech Nienawidzę [chwiejnych] myśli, ale miłuję twoje prawo.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ty jesteś moją ucieczką i tarczą, pokładam nadzieję w twoim słowie.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Odstąpcie ode mnie, złoczyńcy, będę strzegł przykazania mojego Boga.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Wesprzyj mnie według słowa twego, abym żył, i niech nie doznam wstydu ze względu na moją nadzieję.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Podtrzymaj mnie, a będę wybawiony i będę rozmyślał zawsze o twoich prawach.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Podeptałeś wszystkich, którzy odstępują od twoich praw, bo ich zdrada to fałsz.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Odrzucasz [jak] żużel wszystkich niegodziwych ziemi; dlatego miłuję twoje świadectwa.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Moje ciało drży ze strachu przed tobą, bo lękam się twoich sądów.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Ajin Sprawowałem sąd i sprawiedliwość; nie wydawaj mnie moim ciemięzcom.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Bądź poręczycielem dla twego sługi ku dobremu, aby nie uciskali mnie zuchwalcy.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Moje oczy słabną, [czekając] na twoje zbawienie i na słowo twojej sprawiedliwości.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Postąp ze swoim sługą według twego miłosierdzia i naucz mnie twoich praw.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Jestem twoim sługą, daj mi rozum, abym poznał twoje świadectwa.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Już czas, PANIE, abyś działał, [bo] naruszono twoje prawo.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Dlatego umiłowałem twoje przykazania nad złoto, nad szczere złoto.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Bo wszystkie [twoje] przykazania uznaję za prawdziwe, [a] nienawidzę wszelkiej fałszywej drogi.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Pe Twoje świadectwa są przedziwne, dlatego moja dusza ich strzeże.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Początek twoich słów oświeca [i] daje rozum prostym.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Otwieram usta i wzdycham, bo pragnąłem twoich przykazań.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Spójrz na mnie i zmiłuj się nade mną, jak postępujesz z tymi, którzy miłują twoje imię.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Utwierdź moje kroki w twoim słowie, niech nie panuje nade mną żadna nieprawość.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Wybaw mnie z ludzkiego ucisku, abym strzegł twoich nakazów.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Rozjaśnij swe oblicze nad twoim sługą i naucz mnie twoich praw.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Strumienie wód płyną z mych oczu, bo nie strzegą twego prawa.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Cade Sprawiedliwy jesteś, PANIE, i słuszne [są] twoje sądy.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Twoje świadectwa, które nadałeś, są sprawiedliwe i bardzo wierne.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Gorliwość pożarła mnie, bo moi nieprzyjaciele zapominają twoje słowa.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Twoje słowo jest w pełni wypróbowane, dlatego twój sługa je kocha.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Ja jestem mały i wzgardzony, [lecz] nie zapominam twoich przykazań.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Twoja sprawiedliwość jest sprawiedliwością wieczną, a twoje prawo jest prawdą.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Ucisk i utrapienie spadły na mnie, lecz twoje przykazania są moją rozkoszą.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Sprawiedliwość twoich świadectw [trwa] na wieki; daj mi rozum, a będę żył.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Kof Wołam z całego serca, wysłuchaj mnie, o PANIE, a będę strzegł twoich praw.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Wołam do ciebie, wybaw mnie, a będę strzegł twoich świadectw.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Wstaję przed świtem i wołam, oczekuję na twoje słowo.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Moje oczy wyprzedzają straże nocne, abym mógł rozmyślać o twoim słowie.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
PANIE, usłysz mój głos według twego miłosierdzia; ożyw mnie według twego wyroku.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Zbliżają się niegodziwi prześladowcy, są daleko od twego prawa.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Blisko [jesteś], PANIE, i wszystkie twoje przykazania [są] prawdą.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Od dawna wiem o twoich świadectwach, że ugruntowałeś je na wieki.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Resz Wejrzyj na moje utrapienie i wyzwól mnie, bo nie zapomniałem twojego prawa.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Broń mojej sprawy i wybaw mnie; ożyw mnie według twego słowa.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Zbawienie [jest] daleko od niegodziwych, bo nie szukają twoich praw.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Wielka jest twoja litość, PANIE; ożyw mnie według twoich wyroków.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Liczni są moi prześladowcy i nieprzyjaciele; [lecz] nie uchylam się od twoich świadectw.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Widziałem przestępców i czułem odrazę, że nie przestrzegali twego słowa.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Patrz, jak miłuję twoje nakazy, PANIE; ożyw mnie według twego miłosierdzia.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Podstawą twego słowa [jest] prawda, a wszelki wyrok twojej sprawiedliwości [trwa] na wieki.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Szin Władcy prześladują mnie bez przyczyny; moje serce zaś boi się twoich słów.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Raduję się z twego słowa jak ten, który znajduje wielki łup.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Nienawidzę kłamstwa i brzydzę się [nim, ale] miłuję twoje prawo.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Chwalę cię siedem razy dziennie za twoje sprawiedliwe sądy.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Wielki pokój dla tych, którzy miłują twoje prawo, a nie doznają żadnego zgorszenia.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
PANIE, oczekuję na twoje zbawienie i zachowuję twoje przykazania.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Moja dusza przestrzega twoich świadectw, bo bardzo je miłuję.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Przestrzegam twoich przykazań i świadectw, bo wszystkie moje drogi są przed tobą.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Taw PANIE, niech dotrze moje wołanie przed twoje oblicze, daj mi zrozumienie według słowa twego.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Niech dojdzie moja prośba przed twoje oblicze, ocal mnie według twojej obietnicy.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Moje wargi wygłoszą chwałę, gdy nauczysz mnie twoich praw.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Mój język będzie głosił twoje słowo, bo wszystkie twoje przykazania są sprawiedliwością.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Niech twoja ręka będzie mi pomocą, [bo] wybrałem twoje przykazania.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
PANIE, pragnę twego zbawienia, a twoje prawo [jest] moją rozkoszą.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Pozwól mojej duszy żyć, a będzie cię chwalić; niech twoje nakazy będą dla mnie pomocą.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Błądzę jak zgubiona owca; szukaj twego sługi, bo nie zapominam twoich przykazań.

< Masalimo 119 >