< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Alleluia. Blessid ben men with out wem in the weie; that gon in the lawe of the Lord.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blessid ben thei, that seken hise witnessingis; seken him in al the herte.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
For thei that worchen wickidnesse; yeden not in hise weies.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Thou hast comaundid; that thin heestis be kept greetly.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
I wolde that my weies be dressid; to kepe thi iustifiyngis.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Thanne Y schal not be schent; whanne Y schal biholde perfitli in alle thin heestis.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I schal knouleche to thee in the dressing of herte; in that that Y lernyde the domes of thi riytfulnesse.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I schal kepe thi iustifiyngis; forsake thou not me on ech side.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
In what thing amendith a yong waxinge man his weie? in keping thi wordis.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
In al myn herte Y souyte thee; putte thou me not awei fro thin heestis.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
In myn herte Y hidde thi spechis; that Y do not synne ayens thee.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Lord, thou art blessid; teche thou me thi iustifiyngis.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
In my lippis Y haue pronounsid; alle the domes of thi mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I delitide in the weie of thi witnessingis; as in alle richessis.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I schal be ocupied in thin heestis; and Y schal biholde thi weies.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I schal bithenke in thi iustifiyngis; Y schal not foryete thi wordis.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Yelde to thi seruaunt; quiken thou me, and Y schal kepe thi wordis.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Liytne thou myn iyen; and Y schal biholde the merueils of thi lawe.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I am a comeling in erthe; hide thou not thin heestis fro me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mi soule coueitide to desire thi iustifiyngis; in al tyme.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Thou blamedist the proude; thei ben cursid, that bowen awei fro thin heestis.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Do thou awei `fro me schenschipe and dispising; for Y souyte thi witnessingis.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
For whi princis saten, and spaken ayens me; but thi seruaunt was exercisid in thi iustifiyngis.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
For whi and thi witnessyngis is my thenkyng; and my counsel is thi iustifiyngis.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mi soule cleuede to the pawment; quykine thou me bi thi word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I telde out my weies, and thou herdist me; teche thou me thi iustifiyngis.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Lerne thou me the weie of thi iustifiyngis; and Y schal be exercisid in thi merueils.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mi soule nappide for anoye; conferme thou me in thi wordis.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Remoue thou fro me the weie of wickidnesse; and in thi lawe haue thou merci on me.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I chees the weie of treuthe; Y foryat not thi domes.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Lord, Y cleuede to thi witnessyngis; nyle thou schende me.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I ran the weie of thi comaundementis; whanne thou alargidist myn herte.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Lord, sette thou to me a lawe, the weie of thi iustifiyngis; and Y schal seke it euere.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Yyue thou vndurstonding to me, and Y schal seke thi lawe; and Y schal kepe it in al myn herte.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Lede me forth in the path of thin heestis; for Y wolde it.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
`Bowe thou myn herte in to thi witnessingus; and not in to aueryce.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Turne thou awei myn iyen, that `tho seen not vanyte; quykene thou me in thi weie.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Ordeyne thi speche to thi seruaunt; in thi drede.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Kitte awey my schenschip, which Y supposide; for thi domes ben myrie.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Lo! Y coueitide thi comaundementis; quikene thou me in thin equite.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
And, Lord, thi merci come on me; thin heelthe come bi thi speche.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
And Y schal answere a word to men seiynge schenschipe to me; for Y hopide in thi wordis.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
And take thou not awei fro my mouth the word of treuthe outerli; for Y hopide aboue in thi domes.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
And Y schal kepe thi lawe euere; in to the world, and in to the world of world.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
And Y yede in largenesse; for Y souyte thi comaundementis.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
And Y spak of thi witnessyngis in the siyt of kingis; and Y was not schent.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
And Y bithouyte in thin heestis; whiche Y louede.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
And Y reiside myn hondis to thi comaundementis, whiche Y louede; and Y schal be excercisid in thi iustifiyngis.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Lord, haue thou mynde on thi word to thi seruaunt; in which word thou hast youe hope to me.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This coumfortide me in my lownesse; for thi word quikenede me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Proude men diden wickidli bi alle thingis; but Y bowide not awei fro thi lawe.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Lord, Y was myndeful on thi domes fro the world; and Y was coumfortid.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Failing helde me; for synneris forsakinge thi lawe.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Thi iustifiyngis weren delitable to me to be sungun; in the place of my pilgrimage.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Lord, Y hadde mynde of thi name bi niyt; and Y kepte thi lawe.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This thing was maad to me; for Y souyte thi iustifiyngis.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Lord, my part; Y seide to kepe thi lawe.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I bisouyte thi face in al myn herte; haue thou merci on me bi thi speche.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I bithouyte my weies; and Y turnede my feet in to thi witnessyngis.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I am redi, and Y am not disturblid; to kepe thi comaundementis.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
The coordis of synneris han biclippid me; and Y haue not foryete thi lawe.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At mydnyyt Y roos to knouleche to thee; on the domes of thi iustifiyngis.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I am parcener of alle that dreden thee; and kepen thin heestis.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Lord, the erthe is ful of thi merci; teche thou me thi iustifiyngis.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Lord, thou hast do goodnesse with thi seruaunt; bi thi word.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teche thou me goodnesse, and loore, and kunnyng; for Y bileuede to thin heestis.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Bifor that Y was maad meke, Y trespasside; therfor Y kepte thi speche.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Thou art good; and in thi goodnesse teche thou me thi iustifiyngis.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The wickidnesse of hem that ben proude, is multiplied on me; but in al myn herte Y schal seke thin heestis.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
The herte of hem is cruddid as mylk; but Y bithouyte thi lawe.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
It is good to me, that thou hast maad me meke; that Y lerne thi iustifiyngis.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The lawe of thi mouth is betere to me; than thousyndis of gold and of siluer.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Thin hondis maden me, and fourmeden me; yyue thou vndurstondyng to me, that Y lerne thin heestis.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Thei that dreden thee schulen se me, and schulen be glad; for Y hopide more on thi wordis.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Lord, Y knewe, that thi domes ben equite; and in thi treuth thou hast maad me meke.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Thi merci be maad, that it coumforte me; bi thi speche to thi seruaunt.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Thi merciful doyngis come to me, and Y schal lyue; for thi lawe is my thenkyng.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Thei that ben proude be schent, for vniustli thei diden wickidnesse ayens me; but Y schal be exercisid in thin heestis.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Thei that dreden thee be turned to me; and thei that knowen thi witnessyngis.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Myn herte be maad vnwemmed in thi iustifiyngis; that Y be not schent.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mi soule failide in to thin helthe; and Y hopide more on thi word.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Myn iyen failiden in to thi speche; seiynge, Whanne schalt thou coumforte me?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For Y am maad as a bowge in frost; Y haue not foryete thi iustifiyngis.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Hou many ben the daies of thi seruaunt; whanne thou schalt make doom of hem that pursuen me?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Wickid men telden to me ianglyngis; but not as thi lawe.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Alle thi comaundementis ben treuthe; wickid men han pursued me, helpe thou me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Almeest thei endiden me in erthe; but I forsook not thi comaundementis.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Bi thi mersi quikene thou me; and Y schal kepe the witnessingis of thi mouth.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Lord, thi word dwellith in heuene; with outen ende.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Thi treuthe dwellith in generacioun, and in to generacioun; thou hast foundid the erthe, and it dwellith.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
The dai lastith contynueli bi thi ordynaunce; for alle thingis seruen to thee.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
No but that thi lawe was my thenking; thanne perauenture Y hadde perischid in my lownesse.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
With outen ende Y schal not foryete thi iustifiyngis; for in tho thou hast quikened me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I am thin, make thou me saaf; for Y haue souyt thi iustifiyngis.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Synneris aboden me, for to leese me; Y vndurstood thi witnessingis.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
I siy the ende of al ende; thi comaundement is ful large.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Lord, hou louede Y thi lawe; al dai it is my thenking.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Aboue myn enemyes thou madist me prudent bi thi comaundement; for it is to me with outen ende.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I vndurstood aboue alle men techinge me; for thi witnessingis is my thenking.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I vndirstood aboue eelde men; for Y souyte thi comaundementis.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I forbeed my feet fro al euel weie; that Y kepe thi wordis.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I bowide not fro thi domes; for thou hast set lawe to me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Thi spechis ben ful swete to my cheekis; aboue hony to my mouth.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
I vnderstood of thin heestis; therfor Y hatide al the weie of wickidnesse.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Thi word is a lanterne to my feet; and liyt to my pathis.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I swoor, and purposide stidefastli; to kepe the domes of thi riytfulnesse.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I am maad low bi alle thingis; Lord, quykene thou me bi thi word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Lord, make thou wel plesinge the wilful thingis of my mouth; and teche thou me thi domes.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Mi soule is euere in myn hondis; and Y foryat not thi lawe.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Synneris settiden a snare to me; and Y erride not fro thi comaundementis.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
I purchasside thi witnessyngis bi eritage with outen ende; for tho ben the ful ioiyng of myn herte.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I bowide myn herte to do thi iustifiyngis with outen ende; for reward.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
I hatide wickid men; and Y louede thi lawe.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Thou art myn helpere, and my `taker vp; and Y hopide more on thi word.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Ye wickide men, bowe awei fro me; and Y schal seke the comaundementis of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Vp take thou me bi thi word, and Y schal lyue; and schende thou not me fro myn abydyng.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Helpe thou me, and Y schal be saaf; and Y schal bithenke euere in thi iustifiyngis.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Thou hast forsake alle men goynge awey fro thi domes; for the thouyt of hem is vniust.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
I arettide alle the synneris of erthe brekeris of the lawe; therfor Y louede thi witnessyngis.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Naile thou my fleischis with thi drede; for Y dredde of thi domes.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
I dide doom and riytwisnesse; bitake thou not me to hem that falsli chalengen me.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Take vp thi seruaunt in to goodnesse; thei that ben proude chalenge not me.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Myn iyen failiden in to thin helthe; and in to the speche of thi riytfulnesse.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Do thou with thi seruaunt bi thi merci; and teche thou me thi iustifiyngis.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I am thi seruaunt, yyue thou vndurstondyng to me; that Y kunne thi witnessingis.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Lord, it is tyme to do; thei han distried thi lawe.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therfor Y louede thi comaundementis; more than gold and topazion.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therfor Y was dressid to alle thin heestis; Y hatide al wickid weie.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Lord, thi witnessingis ben wondirful; therfor my soule souyte tho.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Declaring of thi wordis liytneth; and yyueth vnderstonding to meke men.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I openede my mouth, and drouy the spirit; for Y desiride thi comaundementis.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Biholde thou on me, and haue merci on me; bi the dom of hem that louen thi name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Dresse thou my goyingis bi thi speche; that al vnriytfulnesse haue not lordschip on me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Ayeyn bie thou me fro the false chalengis of men; that Y kepe thin heestis.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Liytne thi face on thi seruaunt; and teche thou me thi iustifiyngis.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Myn iyen ledden forth the outgoynges of watris; for thei kepten not thi lawe.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Lord, thou art iust; and thi dom is riytful.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Thou hast comaundid riytfulnesse, thi witnessingis; and thi treuthe greetli to be kept.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mi feruent loue made me to be meltid; for myn enemys foryaten thi wordis.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Thi speche is greetli enflawmed; and thi seruaunt louede it.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I am yong, and dispisid; Y foryat not thi iustifiyngis.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Lord, thi riytfulnesse is riytfulnesse with outen ende; and thi lawe is treuthe.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Tribulacioun and angwische founden me; thin heestis is my thenking.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Thi witnessyngis is equite with outen ende; yyue thou vndirstondyng to me, and Y schal lyue.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
I criede in al myn herte, Lord, here thou me; and Y schal seke thi iustifiyngis.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I criede to thee, make thou me saaf; that Y kepe thi comaundementis.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I bifor cam in ripenesse, and Y criede; Y hopide aboue on thi wordis.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Myn iyen bifor camen to thee ful eerli; that Y schulde bithenke thi speches.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Lord, here thou my vois bi thi merci; and quykene thou me bi thi doom.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Thei that pursuen me neiyden to wickidnesse; forsothe thei ben maad fer fro thi lawe.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Lord, thou art nyy; and alle thi weies ben treuthe.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
In the bigynnyng Y knewe of thi witnessingis; for thou hast foundid tho with outen ende.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Se thou my mekenesse, and delyuere thou me; for Y foryat not thi lawe.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Deme thou my dom, and ayenbie thou me; quikene thou me for thi speche.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Heelthe is fer fro synners; for thei souyten not thi iustifiyngis.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Lord, thi mercies ben manye; quykene thou me bi thi dom.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Thei ben manye that pursuen me, and doen tribulacioun to me; Y bowide not awei fro thi witnessingis.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I siy brekers of the lawe, and Y was meltid; for thei kepten not thi spechis.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Lord, se thou, for Y louede thi comaundementis; quikene thou me in thi merci.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
The bigynnyng of thi wordis is treuthe; alle the domes of thi riytwisnesse ben withouten ende.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Princes pursueden me with outen cause; and my herte dredde of thi wordis.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I schal be glad on thi spechis; as he that fyndith many spuylis.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I hatide and wlatide wickidnesse; forsothe Y louede thi lawe.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
I seide heriyngis to thee seuene sithis in the dai; on the domes of thi riytfulnesse.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Miche pees is to hem that louen thi lawe; and no sclaundir is to hem.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Lord, Y abood thin heelthe; and Y louede thin heestis.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mi soule kepte thi witnessyngis; and louede tho greetli.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I kepte thi `comaundementis, and thi witnessingis; for alle my weies ben in thi siyt.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Lord, my biseching come niy in thi siyt; bi thi speche yyue thou vndurstonding to me.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Myn axing entre in thi siyt; bi thi speche delyuere thou me.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mi lippis schulen telle out an ympne; whanne thou hast tauyte me thi iustifiyngis.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Mi tunge schal pronounce thi speche; for whi alle thi comaundementis ben equite.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Thin hond be maad, that it saue me; for Y haue chose thin heestis.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Lord, Y coueitide thin heelthe; and thi lawe is my thenking.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Mi soule schal lyue, and schal herie thee; and thi domes schulen helpe me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I erride as a scheep that perischide; Lord, seke thi seruaunt, for Y foryat not thi comaundementis.

< Masalimo 119 >