< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Blessed are the undefiled in the way, who walk in the law of the LORD.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blessed are they that keep his testimonies, and that seek him with the whole heart.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
They also do no iniquity: they walk in his ways.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Thou hast commanded us to keep thy precepts diligently.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O that my ways were directed to keep thy statutes!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Then shall I not be ashamed, when I have respect to all thy commandments.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I will praise thee with uprightness of heart, when I shall have learned thy righteous judgments.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I will keep thy statutes: O forsake me not utterly.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
How shall a young man cleanse his way? by taking heed to it according to thy word.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
With my whole heart have I sought thee: O let me not wander from thy commandments.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Thy word have I hid in my heart, that I might not sin against thee.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blessed art thou, O LORD: teach me thy statutes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
With my lips have I declared all the judgments of thy mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I have rejoiced in the way of thy testimonies, as much as in all riches.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I will meditate in thy precepts, and have respect to thy ways.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I will delight myself in thy statutes: I will not forget thy word.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Deal bountifully with thy servant, that I may live, and keep thy word.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Open thou my eyes, that I may behold wondrous things out of thy law.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I am a stranger in the earth: hide not thy commandments from me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
My soul breaketh for the longing that it hath to thy judgments at all times.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Thou hast rebuked the proud that are cursed, who do err from thy commandments.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Remove from me reproach and contempt; for I have kept thy testimonies.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Princes also did sit and speak against me: but thy servant did meditate in thy statutes.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Thy testimonies also are my delight and my counsellors.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
My soul cleaveth to the dust: revive thou me according to thy word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I have declared my ways, and thou heardest me: teach me thy statutes.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Make me to understand the way of thy precepts: so shall I talk of thy wondrous works.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
My soul melteth for heaviness: strengthen thou me according to thy word.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Remove from me the way of lying: and grant me thy law graciously.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I have chosen the way of truth: thy judgments have I laid before me.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
I have cleaved to thy testimonies: O LORD, put me not to shame.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I will run the way of thy commandments, when thou shalt enlarge my heart.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Teach me, O LORD, the way of thy statutes; and I shall keep it to the end.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Give me understanding, and I shall keep thy law; yea, I shall observe it with my whole heart.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Make me to go in the path of thy commandments; for in that do I delight.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline my heart to thy testimonies, and not to covetousness.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Turn away my eyes from beholding vanity; and revive thou me in thy way.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Establish thy word to thy servant, who is devoted to thy fear.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Turn away my reproach which I fear: for thy judgments are good.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Behold, I have longed after thy precepts: revive me in thy righteousness.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Let thy mercies come also to me, O LORD, even thy salvation, according to thy word.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
So shall I have that to answer him that reproacheth me: for I trust in thy word.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
And take not the word of truth utterly out of my mouth; for I have hoped in thy judgments.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
So shall I keep thy law continually for ever and ever.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
And I will walk at liberty: for I seek thy precepts.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
I will speak of thy testimonies also before kings, and will not be ashamed.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
And I will delight myself in thy commandments, which I have loved.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
My hands also will I lift to thy commandments, which I have loved; and I will meditate in thy statutes.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Remember the word to thy servant, upon which thou hast caused me to hope.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This is my comfort in my affliction: for thy word hath revived me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
The proud have had me greatly in derision: yet I have not declined from thy law.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
I remembered thy judgments of old, O LORD; and have comforted myself.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Horror hath taken hold upon me because of the wicked that forsake thy law.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Thy statutes have been my songs in the house of my pilgrimage.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
I have remembered thy name, O LORD, in the night, and have kept thy law.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This I had, because I kept thy precepts.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Thou art my portion, O LORD: I have said that I would keep thy words.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I entreated thy favour with my whole heart: be merciful to me according to thy word.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I thought on my ways, and turned my feet to thy testimonies.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I made haste, and delayed not to keep thy commandments.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
The bands of the wicked have robbed me: but I have not forgotten thy law.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At midnight I will rise to give thanks to thee because of thy righteous judgments.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I am a companion of all them that fear thee, and of them that keep thy precepts.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
The earth, O LORD, is full of thy mercy: teach me thy statutes.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Thou hast dealt well with thy servant, O LORD, according to thy word.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teach me good judgment and knowledge: for I have believed thy commandments.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Before I was afflicted I went astray: but now have I kept thy word.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Thou art good, and doest good; teach me thy statutes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The proud have forged a lie against me: but I will keep thy precepts with my whole heart.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Their heart is covered with fat; but I delight in thy law.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
It is good for me that I have been afflicted; that I might learn thy statutes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The law of thy mouth is better to me than thousands of gold and silver.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Thy hands have made me and fashioned me: give me understanding, that I may learn thy commandments.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
They that fear thee will be glad when they see me; because I have hoped in thy word.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
I know, O LORD, that thy judgments are right, and that thou in faithfulness hast afflicted me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Let, I pray thee, thy merciful kindness be for my comfort, according to thy word to thy servant.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Let thy tender mercies come to me, that I may live: for thy law is my delight.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Let the proud be ashamed; for they dealt perversely with me without a cause: but I will meditate in thy precepts.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Let those that fear thee turn to me, and those that have known thy testimonies.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Let my heart be sound in thy statutes; that I may not be ashamed.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
My soul fainteth for thy salvation: but I hope in thy word.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
My eyes fail for thy word, saying, When wilt thou comfort me?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For I am become like a bottle in the smoke; yet I do not forget thy statutes.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
How many are the days of thy servant? when wilt thou execute judgment on them that persecute me?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
The proud have dug pits for me, which are not according to thy law.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
All thy commandments are faithful: they persecute me wrongfully; help thou me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
They had almost consumed me upon earth; but I forsook not thy precepts.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Revive me after thy lovingkindness; so shall I keep the testimony of thy mouth.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
For ever, O LORD, thy word is settled in heaven.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Thy faithfulness is to all generations: thou hast established the earth, and it abideth.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
They continue this day according to thy ordinances: for all are thy servants.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Unless thy law had been my delights, I should then have perished in my affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
I will never forget thy precepts: for with them thou hast revived me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I am thine, save me; for I have sought thy precepts.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
The wicked have waited for me to destroy me: but I will consider thy testimonies.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
I have seen an end of all perfection: but thy commandment is exceeding broad.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
O how I love thy law! it is my meditation all the day.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Thou through thy commandments hast made me wiser than my enemies: for they are ever with me.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I have more understanding than all my teachers: for thy testimonies are my (meditation)
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I understand more than the ancients, because I keep thy precepts.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I have restrained my feet from every evil way, that I might keep thy word.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I have not departed from thy judgments: for thou hast taught me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
How sweet are thy words to my taste! yea, sweeter than honey to my mouth!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Through thy precepts I get understanding: therefore I hate every false way.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Thy word is a lamp to my feet, and a light to my path.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I have sworn, and I will perform it, that I will keep thy righteous judgments.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I am afflicted very much: revive me, O LORD, according to thy word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Accept, I beseech thee, the freewill offerings of my mouth, O LORD, and teach me thy judgments.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
My soul is continually in my hand: yet I do not forget thy law.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
The wicked have laid a snare for me: yet I erred not from thy precepts.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Thy testimonies have I taken as an heritage for ever: for they are the rejoicing of my heart.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I have inclined my heart to perform thy statutes always, even to the end.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate vain thoughts: but thy law do I love.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Thou art my hiding place and my shield: I hope in thy word.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Depart from me, ye evildoers: for I will keep the commandments of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uphold me according to thy word, that I may live: and let me not be ashamed of my hope.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Support me, and I shall be safe: and I will have respect to thy statutes continually.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Thou hast trodden down all them that err from thy statutes: for their deceit is falsehood.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Thou puttest away all the wicked of the earth like dross: therefore I love thy testimonies.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
My flesh trembleth for fear of thee; and I am afraid of thy judgments.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
I have executed justice and righteousness: leave me not to my oppressors.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Be surety for thy servant for good: let not the proud oppress me.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
My eyes fail for thy salvation, and for the word of thy righteousness.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Deal with thy servant according to thy mercy, and teach me thy statutes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I am thy servant; give me understanding, that I may know thy testimonies.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
It is time for thee, LORD, to work: for they have made void thy law.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therefore I love thy commandments above gold; yea, above fine gold.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therefore I esteem all thy precepts concerning all things to be right; and I hate every false way.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Thy testimonies are wonderful: therefore doth my soul keep them.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
The entrance of thy words giveth light; it giveth understanding to the simple.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I opened my mouth, and panted: for I longed for thy commandments.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Look thou upon me, and be merciful to me, as thou didst use to do to those that love thy name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Order my steps in thy word: and let not any iniquity have dominion over me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Deliver me from the oppression of man: so will I keep thy precepts.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Make thy face to shine upon thy servant; and teach me thy statutes.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Rivers of waters run down my eyes, because they keep not thy law.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Righteous art thou, O LORD, and upright are thy judgments.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Thy testimonies that thou hast commanded are righteous and very faithful.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
My zeal hath consumed me, because my enemies have forgotten thy words.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Thy word is very pure: therefore thy servant loveth it.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I am small and despised: yet I do not forget thy precepts.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Thy righteousness is an everlasting righteousness, and thy law is the truth.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Trouble and anguish have taken hold on me: yet thy commandments are my delights.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
The righteousness of thy testimonies is everlasting: give me understanding, and I shall live.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
I cried with my whole heart; hear me, O LORD: I will keep thy statutes.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I cried to thee; save me, and I shall keep thy testimonies.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I came before the dawning of the morning, and cried: I hoped in thy word.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
My eyes are awake through the night watches, that I might meditate in thy word.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hear my voice according to thy lovingkindness: O LORD, revive me according to thy judgment.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
They draw near that follow after mischief: they are far from thy law.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Thou art near, O LORD; and all thy commandments are truth.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Concerning thy testimonies, I have known of old that thou hast founded them for ever.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Consider my affliction, and deliver me: for I do not forget thy law.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plead my cause, and deliver me: revive me according to thy word.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Salvation is far from the wicked: for they seek not thy statutes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Great are thy tender mercies, O LORD: revive me according to thy judgments.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Many are my persecutors and my enemies; yet I do not decline from thy testimonies.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I beheld the transgressors, and was grieved; because they kept not thy word.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Consider how I love thy precepts: revive me, O LORD, according to thy lovingkindness.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Thy word is true from the beginning: and every one of thy righteous judgments endureth for ever.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Princes have persecuted me without a cause: but my heart standeth in awe of thy word.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I rejoice at thy word, as one that findeth great spoil.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate and abhor lying: but thy law do I love.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seven times a day do I praise thee because of thy righteous judgments.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Great peace have they who love thy law: and nothing shall cause them to stumble.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
LORD, I have hoped for thy salvation, and performed thy commandments.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
My soul hath kept thy testimonies; and I love them exceedingly.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I have kept thy precepts and thy testimonies: for all my ways are before thee.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Let my cry come near before thee, O LORD: give me understanding according to thy word.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Let my supplication come before thee: deliver me according to thy word.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
My lips shall utter praise, when thou hast taught me thy statutes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
My tongue shall speak of thy word: for all thy commandments are righteousness.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Let thy hand help me; for I have chosen thy precepts.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
I have longed for thy salvation, O LORD; and thy law is my delight.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Let my soul live, and it shall praise thee; and let thy judgments help me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I have gone astray like a lost sheep; seek thy servant; for I do not forget thy commandments.

< Masalimo 119 >