< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
J’aime l’Éternel, car il entend Ma voix, mes supplications;
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Car il a penché son oreille vers moi; Et je l’invoquerai toute ma vie.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
Les liens de la mort m’avaient environné, Et les angoisses du sépulcre m’avaient saisi; J’étais en proie à la détresse et à la douleur. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Mais j’invoquai le nom de l’Éternel: O Éternel, sauve mon âme!
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
L’Éternel est miséricordieux et juste, Notre Dieu est plein de compassion;
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
L’Éternel garde les simples; J’étais malheureux, et il m’a sauvé.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Mon âme, retourne à ton repos, Car l’Éternel t’a fait du bien.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Oui, tu as délivré mon âme de la mort, Mes yeux des larmes, Mes pieds de la chute.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Je marcherai devant l’Éternel, Sur la terre des vivants.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
J’avais confiance, lorsque je disais: Je suis bien malheureux!
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Je disais dans mon angoisse: Tout homme est trompeur.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Comment rendrai-je à l’Éternel Tous ses bienfaits envers moi?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
J’élèverai la coupe des délivrances, Et j’invoquerai le nom de l’Éternel;
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
J’accomplirai mes vœux envers l’Éternel, En présence de tout son peuple.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Elle a du prix aux yeux de l’Éternel, La mort de ceux qui l’aiment.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Écoute-moi, ô Éternel! Car je suis ton serviteur, Ton serviteur, fils de ta servante. Tu as détaché mes liens.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Je t’offrirai un sacrifice d’actions de grâces, Et j’invoquerai le nom de l’Éternel;
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
J’accomplirai mes vœux envers l’Éternel, En présence de tout son peuple,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Dans les parvis de la maison de l’Éternel, Au milieu de toi, Jérusalem! Louez l’Éternel!

< Masalimo 116 >