< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Alleluia. I am well pleased, because the Lord will listen to the voice of my supplication.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Because he has inclined his ear to me, therefore will I call upon him while I live.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
The pangs of death compassed me; the dangers of hell found me: I found affliction and sorrow. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Then I called on the name of the Lord: O Lord, deliver my soul.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
The Lord is merciful and righteous; yes, our God has pity.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
The Lord preserves the simple: I was brought low, and he delivered me.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Return to your rest, O my soul; for the Lord has dealt bountifully with you.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
For he has delivered my soul from death, mine eyes from tears, and my feet from falling.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I shall be well-pleasing before the Lord in the land of the living.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Alleluia. I believed, therefore I have spoken: but I was greatly afflicted.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
And I said in mine amazement, Every man is a liar.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
What shall I render to the Lord for all the things wherein he has rewarded me?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
I will take the cup of salvation, and call upon the name of the Lord.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
I will pay my vows to the Lord, in the presence of all his people.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Precious in the sight of the Lord is the death of his saints.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
O Lord, I am your servant; I am your servant, and the son of your handmaid: you have burst by bonds asunder.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
I will offer to you the sacrifice of praise, and will call upon the name of the Lord.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
I will pay my vows to the Lord, in the presence of all his people,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
in the courts of the Lord's house, in the midst of you, Jerusalem.

< Masalimo 116 >