< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ne nama, Gospode, ne nama, nego imenu svojemu daj slavu, po milosti svojoj, po istini svojoj.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Zašto da govore narodi: gdje li je Bog njihov?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Bog je naš na nebesima, tvori sve što hoæe.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Idoli su njihovi srebro i zlato, djelo ruku èovjeèijih.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Usta imaju, a ne govore; oèi imaju, a ne vide;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
Uši imaju, a ne èuju; nozdrve imaju, a ne mirišu;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Ruke imaju, a ne hvataju; noge imaju, a ne hode, i ne puštaju glasa iz grla svojega.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Taki su i oni koji ih grade, i svi koji se uzdaju u njih.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Dome Izrailjev, uzdaj se u Gospoda; on im je pomoæ i štit.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Dome Aronov, uzdaj se u Gospoda; on im je pomoæ i štit.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Koji se bojite Gospoda, uzdajte se u Gospoda; on im je pomoæ i štit.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
Gospod nas se opominje, blagosilja nas, blagosilja dom Izrailjev, blagosilja dom Aronov;
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
Blagosilja one koji se boje Gospoda, male i velike.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Da vam Gospod umnoži blagoslove, vama i sinovima vašim!
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Gospod da vas blagoslovi, tvorac neba i zemlje!
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Nebo je nebo Gospodnje, a zemlju je dao sinovima èovjeèijim.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Neæe te mrtvi hvaliti, Gospode, niti oni koji siðu onamo gdje se muèi.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Nego æemo mi blagosiljati Gospoda otsad i dovijeka. Aliluja!

< Masalimo 115 >