< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Hallelujah! Lobet, ihr Knechte Jehovahs, lobet Jehovahs Namen!
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Jehovahs Name sei gesegnet von nun an und bis in Ewigkeit!
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Vom Aufgang der Sonne bis zu ihrem Niedergang sei gelobt Jehovahs Name!
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Erhöht über alle Völkerschaften ist Jehovah, über die Himmel Seine Herrlichkeit.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Wer ist wie Jehovah, unser Gott, Der hoch macht Seinen Sitz.
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Der Sich erniedrigt, zu sehen in die Himmel und die Erde.
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Der aus dem Staub aufrichtet den Armen, von dem Düngerhaufen erhöht den Dürftigen,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Daß Er ihn lasse sitzen mit den Edlen, mit den Edlen Seines Volkes.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Der die Unfruchtbare läßt im Hause wohnen, eine frohe Mutter von Söhnen. Hallelujah!

< Masalimo 113 >