< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Blago èovjeku koji se boji Gospoda, kome su veoma omiljele zapovijesti njegove.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Silno æe biti na zemlji sjeme njegovo, rod pravednièki biæe blagosloven.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Obilje je i bogatstvo u domu njegovu, i pravda njegova traje dovijeka.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
U tami sjaje vidjelo pravednicima od dobroga, milostivoga i pravednoga.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Blago onome koji je milostiv i daje u zajam! On æe dati tvrðu rijeèima svojim na sudu.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Jer neæe posrnuti dovijeka, pravednik æe se spominjati uvijek.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Ne boji se zla glasa; srce je njegovo stalno, uzda se u Gospoda.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Utvrðeno je srce njegovo, neæe se pobojati, i vidjeæe kako padaju neprijatelji njegovi.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Prosipa, daje ubogima; pravda njegova traje dovijeka, rog se njegov uzvišuje u slavi.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Bezbožnik vidi i jedi se, škrguæe zubima svojim, i sahne. Želja æe bezbožnicima propasti.

< Masalimo 112 >