< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Gotovo je srce moje, Bože; pjevaæu i hvaliæu zajedno sa slavom svojom.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Preni se psaltire i gusle, ustaæu rano.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Slaviæu tebe, Gospode, po narodima, pojaæu tebi po plemenima.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Jer je svrh nebesa milost tvoja i do oblaka istina tvoja.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Uzvisi se više nebesa, Bože, i po svoj zemlji neka bude slava tvoja!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Da bi se izbavili mili tvoji, pomozi desnicom svojom, i usliši me.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Bog reèe u svetinji svojoj: “veseliæu se, razdijeliæu Sihem, i dolinu Sokot razmjeriæu.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Moj je Galad, moj je Manasija, Jefrem je krjepost glave moje, Juda skiptar moj.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moav je èaša iz koje se umivam, Edomu æu pružiti obuæu svoju; nad zemljom Filistejskom popijevaæu.”
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Ko æe me odvesti u tvrdi grad? ko æe me otpratiti do Edoma?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Zar neæeš ti, Bože, koji si nas odbacio, i ne ideš, Bože, s vojskama našim?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Daj nam pomoæ u tjeskobi, obrana je èovjeèija uzalud.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Bogom smo jaki; on gazi neprijatelje naše.

< Masalimo 108 >