< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Hvalite Gospoda; glasite ime njegovo; javljajte po narodima djela njegova.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Pjevajte mu i slavite ga; kazujte sva èudesa njegova.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Hvalite se svetijem imenom njegovijem; nek se veseli srce onijeh koji traže Gospoda.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Tražite Gospoda i silu njegovu, tražite lice njegovo bez prestanka.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Pamtite èudesa njegova koja je uèinio, znake njegove i sudove usta njegovijeh.
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
Sjeme Avramovo sluge su njegove, sinovi Jakovljevi izbrani njegovi.
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
On je Gospod Bog naš, po svoj su zemlji sudovi njegovi.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Pamti uvijek zavjet svoj, rijeè, koju je dao na tisuæu koljena,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
Što je zavjetovao Avramu, i za što se kleo Isaku.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
To je postavio Jakovu za zakon, i Izrailju za zavjet vjeèni,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Govoreæi: tebi æu dati zemlju Hanansku u našljedni dio.
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Tada ih još bijaše malo na broj, bijaše ih malo, i bjehu došljaci.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
Iðahu od naroda do naroda, iz jednoga carstva k drugome plemenu.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Ne dade nikome da im naudi, i karaše za njih careve:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
“Ne dirajte u pomazanike moje, i prorocima mojim ne èinite zla.”
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
I pusti glad na onu zemlju; i potr sav hljeb što je za hranu.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Posla pred njima èovjeka; u roblje prodan bi Josif.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Okovima stegoše noge njegove, gvožðe tištaše dušu njegovu,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Dok se steèe rijeè njegova, i rijeè Gospodnja proslavi ga.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Posla car i odriješi ga; gospodar nad narodima, i pusti ga.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Postavi ga gospodarem nad domom svojim, i zapovjednikom nad svijem što imaše.
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
Da vlada nad knezovima njegovijem po svojoj volji, i starješine njegove urazumljuje.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Tada doðe Izrailj u Misir, i Jakov se preseli u zemlju Hamovu.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
I namnoži Bog narod svoj i uèini ga jaèega od neprijatelja njegovijeh.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Prevrnu se srce njihovo te omrznuše na narod njegov, i èiniše lukavstvo slugama njegovijem.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Posla Mojsija, slugu svojega, Arona izbranika svojega.
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Pokazaše meðu njima èudotvornu silu njegovu i znake njegove u zemlji Hamovoj.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Pusti mrak i zamraèi, i ne protiviše se rijeèi njegovoj.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Pretvori vodu njihovu u krv, i pomori ribu njihovu.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Provre zemlja njihova žabama, i klijeti careva njihovijeh.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Reèe, i doðoše bubine, uši po svijem krajevima njihovijem.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Mjesto dažda posla na njih grad, živi oganj na zemlju njihovu.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
I pobi èokote njihove i smokve njihove, i potr drveta u krajevima njihovijem.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Reèe, i doðoše skakavci i gusjenice nebrojene;
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
I izjedoše svu travu po zemlji njihovoj, i pojedoše rod u polju njihovu.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
I pobi sve prvence u zemlji njihovoj, prvine svakoga truda njihova.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Izvede Izrailjce sa srebrom i zlatom, i ne bješe sustala u plemenima njihovijem.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Obradova se Misir izlasku njihovu, jer strah njihov bješe na nj pao.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Razastrije im oblak za pokrivaè, i oganj da svijetli noæu.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Moliše, i posla im prepelice, i hljebom ih nebeskim hrani.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Otvori kamen i proteèe voda, rijeke protekoše po suhoj pustinji.
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Jer se opominjaše svete rijeèi svoje k Avramu, sluzi svojemu.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
I izvede narod svoj u radosti, izbrane svoje u veselju.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
I dade im zemlju naroda i trud tuðinaca u našljedstvo.
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
Da bi èuvali zapovijesti njegove, i zakone njegove pazili. Aliluja.

< Masalimo 105 >