< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Wysławiajcie PANA, wzywajcie jego imienia, opowiadajcie jego dzieła wśród narodów.
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Śpiewajcie mu, śpiewajcie mu psalmy, rozmawiajcie o wszystkich jego cudach.
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Chlubcie się jego świętym imieniem, niech się weseli serce szukających PANA.
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Szukajcie PANA i jego mocy, szukajcie zawsze jego oblicza.
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Przypominajcie sobie dzieła, które czynił; jego cuda i wyroki jego ust.
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
[Wy], potomkowie Abrahama, jego słudzy; [wy], synowie Jakuba, jego wybrańcy!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
On jest PANEM, naszym Bogiem, jego sądy po całej ziemi.
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Pamięta wiecznie o swoim przymierzu; o słowie, które nakazał po tysiąc pokoleń;
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
[O przymierzu], które zawarł z Abrahamem, i o przysiędze złożonej Izaakowi.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Ustanowił je jako prawo dla Jakuba, dla Izraela jako wieczne przymierze;
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
Mówiąc: Tobie dam ziemię Kanaan jako dział waszego dziedzictwa;
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Kiedy ich było niewielu, nieliczni i obcy w niej.
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
I wędrowali od narodu do narodu, z [jednego] królestwa do innego ludu;
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Nikomu nie pozwolił ich krzywdzić, nawet karcił królów z ich powodu, [mówiąc]:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
Nie dotykajcie moich pomazańców, a moim prorokom nie czyńcie [nic] złego.
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
Potem przywołał głód na ziemię i zniszczył cały zapas chleba.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Posłał przed nimi męża, Józefa, który został sprzedany jako niewolnik;
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Którego nogi ranili pętami, a w żelazo zakuto jego ciało;
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
Aż do [tego] czasu, gdy jego słowo się spełniło, słowo PANA doświadczało go.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Posłał król i kazał go uwolnić, władca narodu wypuścił go na wolność.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Ustanowił go panem swego domu i władcą wszystkich swoich posiadłości;
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
Aby rządził jego dostojnikami według swego uznania i jego starszych nauczał mądrości.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
Potem Izrael wszedł do Egiptu, a Jakub był gościem w ziemi Chama;
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
Gdzie [Bóg] bardzo rozmnożył swój lud i uczynił go potężniejszym od jego wrogów.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Odmienił ich serca, żeby znienawidzili jego lud i postępowali przebiegle wobec jego sług.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Posłał Mojżesza, swego sługę, i Aarona, którego wybrał;
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
Pokazali im jego znaki i cuda w ziemi Chama.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Zesłał ciemności i nastał mrok, i nie buntowali się przeciw jego słowu.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Zamienił ich wody w krew i pozabijał ich ryby.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Ich ziemia wydała mnóstwo żab, [były] nawet w komnatach królewskich.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Rozkazał i zjawiły się rozmaite muchy i wszy w całym ich kraju.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Zesłał grad zamiast deszczu, ogień płonący na ich ziemię.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
Zniszczył ich winnice i figowce i połamał drzewa w ich kraju.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Rozkazał i zjawiła się szarańcza, niezliczone mnóstwo larw;
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
I pożarły całą zieleń w ich kraju, i zjadły płody ich ziemi.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
Zabił też wszystko, co pierworodne w ich ziemi, pierwociny wszelkiej ich siły.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
Wyprowadził ich ze srebrem i złotem i nie było słabego wśród ich plemion.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Egipt się radował, gdy wychodzili, bo ogarnął go strach przed nimi.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Rozpostarł obłok jak osłonę, a ogień, by świecił w nocy.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Na [ich] żądanie zesłał przepiórki i nasycił ich chlebem z nieba.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Otworzył skałę i trysnęły wody, popłynęły po suchych miejscach [jak] rzeka;
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
Pamiętał bowiem o swoim świętym słowie i o Abrahamie, swym słudze.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
Wyprowadził swój lud wśród wesela, swoich wybranych wśród radości.
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
I dał im ziemię pogan, i zawładnęli dorobkiem narodów;
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
Aby zachowywali jego nakazy i przestrzegali jego praw. Alleluja.

< Masalimo 105 >