< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Błogosław, moja duszo, PANA. PANIE, mój Boże, jesteś bardzo wielki; odziałeś się w chwałę i majestat.
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
Okryłeś się światłością jak szatą, rozciągnąłeś niebiosa jak zasłonę.
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
Zbudowałeś na wodach swoje komnaty, czynisz obłoki swym rydwanem, chodzisz na skrzydłach wiatru.
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
Czynisz swoich aniołów duchami, swe sługi ogniem płonącym.
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
Założyłeś fundamenty ziemi, tak że się nigdy nie zachwieje.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Okryłeś ją głębią jak szatą, wody stanęły nad górami.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
Na twoje zgromienie rozbiegły się, a na głos twego grzmotu szybko pouciekały.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
Wzniosły się ponad góry, zniżyły się w doliny, na miejsce, które dla nich założyłeś.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Wyznaczyłeś [im] granicę, aby jej nie przekroczyły ani nie powróciły, by okryć ziemię.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
Wypuszczasz źródła po dolinach, [aby] płynęły między górami;
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
I napoiły wszystkie zwierzęta polne, dzikie osły gaszą [w nich] swoje pragnienie.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
Przy nich mieszka ptactwo niebieskie i śpiewa pośród gałęzi.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
Nawadniasz góry ze swoich komnat, owocami twoich dzieł syci się ziemia.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
Sprawiasz, że rośnie trawa dla bydła i zioła na użytek człowieka, żeby dobywał chleb z ziemi;
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
I wino, które rozwesela serce człowieka, i oliwę, od której rozjaśnia się twarz, i chleb, który krzepi serce ludzkie.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
Nasycone są drzewa PANA, cedry Libanu, które zasadził;
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
Na których ptaki mają swe gniazda; jedliny, na których bocian [ma] swój dom.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
Wysokie góry są dla górskich kozłów, a skały [są] schronieniem dla królików.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
Uczynił księżyc, aby odmierzał czas; słońce zna swój zachód.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Sprowadzasz ciemność i nastaje noc, w której wychodzą wszystkie zwierzęta leśne.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
Lwiątka ryczą za łupem i szukają swego pokarmu od Boga.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
Słońce wstaje, schodzą się razem i kładą się w swoich jamach.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
[Wtedy] wychodzi człowiek do swojej roboty i do swojej pracy aż do wieczora.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
O, jak liczne są twoje dzieła, PANIE! Wszystkie je uczyniłeś mądrze, ziemia jest pełna twego bogactwa.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Oto morze wielkie i szerokie, w nim niezliczone istoty pełzające, zwierzęta małe i wielkie.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
Po nim pływają okręty i Lewiatan, którego stworzyłeś, aby w nim igrał.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
Wszystko to czeka na ciebie, abyś dał im pokarm we właściwym czasie.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
[Gdy] dajesz im, zbierają; gdy otwierasz swą rękę, sycą się dobrami.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
[Lecz gdy] ukrywasz swe oblicze, trwożą się; gdy odbierasz im ducha, giną i obracają się w proch.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
[Gdy] wysyłasz twego ducha, zostają stworzone i odnawiasz oblicze ziemi.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Niech chwała PANA trwa na wieki, niech się raduje PAN swymi dziełami.
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
Patrzy na ziemię, a ona drży, dotyka gór, a dymią.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
Będę śpiewał PANU, póki żyję; będę śpiewał memu Bogu, póki istnieję.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Moje rozmyślanie o nim wdzięczne będzie, rozraduję się w PANU.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Niech zostaną wytraceni z ziemi grzesznicy i niech nie będzie już niegodziwych! Błogosław, moja duszo, PANA. Alleluja.

< Masalimo 104 >