< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Psalm Dawida. Błogosław, moja duszo, PANA, i całe moje wnętrze – jego święte imię.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Błogosław, moja duszo, PANA, i nie zapominaj o wszystkich jego dobrodziejstwach.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
On przebacza wszystkie twoje nieprawości, on uzdrawia wszystkie twoje choroby;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
On wybawia twoje życie od zguby, on cię koronuje miłosierdziem i wielką litością.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
On nasyca dobrem twoje usta i odnawia twoją młodość jak u orła.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
PAN wymierza sprawiedliwość i sąd wszystkim uciśnionym.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Dał poznać swe drogi Mojżeszowi, a synom Izraela swoje dzieła.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Łaskawy i litościwy jest PAN, nieskory do gniewu i [pełen] wielkiego miłosierdzia.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Nie będzie się spierał bez końca ani wiecznie [gniewu] chował.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Nie postępuje z nami według naszych grzechów ani nie odpłaca nam według naszych nieprawości.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Jak wysoko bowiem są niebiosa nad ziemią, [tak] wielkie [jest] jego miłosierdzie nad tymi, którzy się go boją.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Jak daleko jest wschód od zachodu, [tak] daleko oddalił od nas nasze występki.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Jak ojciec ma litość nad dziećmi, tak PAN ma litość nad tymi, którzy się go boją.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
On bowiem wie, z czego jesteśmy ulepieni; pamięta, że jesteśmy prochem.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
Dni człowieka są jak trawa, kwitnie jak kwiat polny.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
Wiatr na niego powieje, a już go nie ma i nie pozna go już jego miejsce.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Ale miłosierdzie PANA od wieków na wieki nad tymi, którzy się go boją, a jego sprawiedliwość nad synami synów;
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
[Nad tymi], którzy strzegą jego przymierza i pamiętają, aby wypełnić jego przykazania.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
PAN na niebiosach ustanowił [swój] tron, a jego królestwo panuje nad wszystkimi.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Błogosławcie PANA, jego aniołowie, potężni siłą, którzy wypełniacie jego rozkazy, będąc posłuszni głosowi jego słowa.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Błogosławcie PANA, wszystkie jego zastępy, jego słudzy, którzy spełniacie jego wolę.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Błogosławcie PANA, wszystkie jego dzieła, we wszystkich miejscach jego panowania. Błogosław, moja duszo, PANA.

< Masalimo 103 >