< Masalimo 1 >

1 Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Blessed is the man that walketh not in the counsel of the ungodly, nor standeth in the way of sinners, nor sitteth in the seat of scoffers.
2 Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
But his delight is in the law of the LORD; and in his law doth he meditate day and night.
3 Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
And he shall be like a tree planted by the rivers of water, that bringeth forth its fruit in its season; its leaf also shall not wither; and whatever he doeth shall prosper.
4 Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
The ungodly are not so: but are like the chaff which the wind driveth away.
5 Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
Therefore the ungodly shall not stand in the judgment, nor sinners in the congregation of the righteous.
6 Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
For the LORD knoweth the way of the righteous: but the way of the ungodly shall perish.

< Masalimo 1 >