< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Proverbios de Salomão, filho de David, rei d'Israel;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Para se conhecer a sabedoria e a instrucção; para se entenderem as palavras da prudencia;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Para se receber a instrucção do entendimento, a justiça, o juizo, e a equidade;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Para dar aos simplice prudencia, e aos moços conhecimento e bom siso;
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Para o sabio ouvir e crescer em doutrina, e o entendido adquirir sabios conselhos;
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Para entender proverbios e a sua declaração: como tambem as palavras dos sabios, e as suas adivinhações.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
O temor do Senhor é o principio da sciencia: os loucos desprezam a sabedoria e a instrucção.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Filho meu, ouve a instrucção de teu pae, e não deixes a doutrina de tua mãe.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Porque diadema de graça serão para a tua cabeça, e colares para o teu pescoço.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Filho meu, se os peccadores te attrahirem com afagos, não consintas.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Se disserem: Vem comnosco; espiemos o sangue; espreitemos o innocente sem razão;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Traguemol-os vivos, como a sepultura; e inteiros, como os que descem á cova; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Acharemos toda a sorte de fazenda preciosa; encheremos as nossas casas de despojos;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Lança a tua sorte entre nós; teremos todos uma só bolsa.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Filho meu, não te ponhas a caminho com elles: desvia o pé das suas veredas;
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Porque os seus pés correm para o mal, e se apressam a derramar sangue.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Na verdade debalde se estende a rede perante os olhos de toda a sorte d'aves.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
E estes armam ciladas contra o seu proprio sangue; e as suas proprias vidas espreitam.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Assim são as veredas de todo aquelle que usa d'avareza: ella prenderá a alma de seus amos.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
A suprema sabedoria altamente clama de fóra: pelas ruas levanta a sua voz.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Nas encruzilhadas, em que ha tumultos, clama: ás entradas das portas, na cidade profere as suas palavras.
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Até quando, ó simplices, amareis a simplicidade? e vós, escarnecedores, desejareis o escarneo? e vós, loucos, aborrecereis o conhecimento?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Tornae-vos á minha reprehensão: eis que abundantemente vos derramarei de meu espirito e vos farei saber as minhas palavras.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Porquanto clamei, e vós recusastes; estendi a minha mão, e não houve quem désse attenção;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Mas rejeitastes todo o meu conselho, e não quizestes a minha reprehensão.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Tambem eu me rirei na vossa perdição, e zombarei, vindo o vosso temor;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Vindo como a assolação o vosso temor, e vindo a vossa perdição como uma tormenta, sobrevindo-vos aperto e angustia.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Então a mim clamarão, porém eu não responderei; de madrugada me buscarão, porém não me acharão.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Porquanto aborreceram o conhecimento; e não elegeram o temor do Senhor;
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Não consentiram ao meu conselho e desprezaram toda a minha reprehensão.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Assim que comerão do fructo do seu caminho, e fartar-se-hão dos seus proprios conselhos.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Porque o desvio dos simplices os matará, e a prosperidade dos loucos os destruirá.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Porém o que me der ouvidos habitará seguramente, e estará descançado do temor do mal

< Miyambo 1 >