< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Sine, èuvaj rijeèi moje, i zapovijesti moje sahrani kod sebe.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Èuvaj zapovijesti moje i biæeš živ, i nauku moju kao zjenicu oèiju svojih.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Priveži ih sebi na prste, napiši ih na ploèi srca svojega.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Reci mudrosti: sestra si mi; i prijateljicom zovi razboritost,
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Da bi te èuvala od žene tuðe, od tuðinke, koja laska rijeèima.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Jer s prozora doma svojega kroz rešetku gledah,
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
I vidjeh meðu ludima, opazih meðu djecom bezumna mladiæa,
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Koji iðaše ulicom pokraj ugla njezina, i koraèaše putem ka kuæi njezinoj,
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
U sumrak, uveèe, kad se unoæa i smrèe;
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
A gle, srete ga žena u odijelu kurvinskom i lukava srca,
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Plaha i pusta, kojoj noge ne mogu stajati kod kuæe,
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Sad na polju, sad na ulici, kod svakoga ugla vrebaše.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
I uhvati ga, i poljubi ga, i bezobrazno reèe mu:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
Imam žrtve zahvalne, danas izvrših zavjete svoje;
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Zato ti izidoh na susret da te tražim, i naðoh te.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Nastrla sam odar svoj pokrivaèima vezenijem i prostirkama Misirskim.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
Okadila sam postelju svoju smirnom, alojem i cimetom.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Hajde da se opijamo ljubavlju do zore, da se veselimo milovanjem.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Jer mi muž nije kod kuæe, otišao je na put daljni,
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Uzeo je sa sobom tobolac novèani, vratiæe se kuæi u odreðeni dan.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Navrati ga mnogim rijeèima, glatkim usnama odvuèe ga.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Otide za njom odmah kao što vo ide na klanje i kao bezumnik u puto da bude karan,
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Dokle mu strijela ne probije jetru, kao što ptica leti u zamku ne znajuæi da joj je o život.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Zato dakle, djeco, poslušajte me, i pazite na rijeèi usta mojih.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Nemoj da zastranjuje srce tvoje na putove njezine, nemoj lutati po stazama njezinijem.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Jer je mnoge ranila i oborila, i mnogo je onijeh koje je sve pobila.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Kuæa je njezina put pakleni koji vodi u klijeti smrtne. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >