< Miyambo 7 >

1 Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
Synu mój, strzeż moich słów i przechowuj u siebie moje przykazania.
2 Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Strzeż moich przykazań, a będziesz żył; [strzeż] mojego prawa jak źrenicy swych oczu.
3 Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Przywiąż je do swoich palców, wypisz je na tablicy twego serca.
4 Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Mów do mądrości: Jesteś moją siostrą, a roztropność nazywaj przyjaciółką;
5 Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
Aby cię strzegły przed cudzą żoną i przed obcą, [która] mówi gładkie słowa.
6 Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
Bo z okna swego domu wyglądałem przez kratę;
7 Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
I zobaczyłem wśród prostych, zauważyłem wśród chłopców nierozumnego młodzieńca;
8 Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Który przechodził ulicą blisko jej narożnika, idąc drogą do jej domu.
9 Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
O zmierzchu, pod wieczór, w ciemności nocnej i w mroku.
10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
A oto spotkała go kobieta w stroju nierządnicy, chytrego serca;
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
Wrzaskliwa i nieopanowana, której nogi nie mogą pozostać w domu:
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
Raz na dworze, raz na ulicach i czyha na każdym rogu.
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
Chwyciła go i pocałowała, z bezczelną miną powiedziała do niego:
14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
U mnie są ofiary pojednawcze; spełniłam dzisiaj swoje śluby.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
Dlatego wyszłam ci naprzeciw, szukałam pilnie twojej twarzy i znalazłam cię.
16 Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
Obiłam kobiercami swoje łoże, [przystrojone] rzeźbieniem i prześcieradłami z Egiptu.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
Skropiłam swoje posłanie mirrą, aloesem i cynamonem.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
Chodź, upójmy się miłością aż do rana, nacieszmy się miłością.
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
Bo [mojego] męża nie ma w domu; pojechał w daleką drogę.
20 Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
Wziął ze sobą worek pieniędzy; umówionego dnia wróci do domu.
21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
Nakłoniła go mnóstwem swoich słów i zniewoliła go pochlebstwem swoich warg.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
Wnet poszedł za nią jak wół prowadzony na rzeź i jak głupi na karę pęt.
23 mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
Aż strzała przebije mu wątrobę; spieszy jak ptak w sidła, nie wiedząc, że [chodzi] o jego życie.
24 Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
Więc teraz słuchajcie mnie, synowie, i zważajcie na słowa moich ust.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
Niech twoje serce nie zbacza na jej drogi i nie tułaj się po jej ścieżkach.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
Bo wielu zranionych strąciła i wielu mocarzy pozabijała.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)
Jej dom [jest] drogą do piekła, która wiedzie do komnat śmierci. (Sheol h7585)

< Miyambo 7 >