< Miyambo 31 >

1 Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
Rijeèi cara Lemuila; sabrane rijeèi, kojima ga je uèila mati njegova.
2 Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
Šta, sine moj, šta, sine utrobe moje, i šta, sine zavjeta mojih?
3 Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
Ne daj krjeposti svoje ženama, ni putova svojih onima što satiru careve.
4 Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
Nije za careve, Lemuilo, nije za careve da piju vino, ni za knezove da piju silovito piæe,
5 kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
Da ne bi pijuæi zaboravio uredbe, i izmijenio pravicu kojemu nevoljniku.
6 Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
Podajte silovito piæe onome koji hoæe da propadne, i vino onima koji su tužna srca;
7 amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
Neka se napije i zaboravi svoje siromaštvo, i da se više ne sjeæa svoje muke.
8 Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
Otvoraj usta svoja za nijemoga, za stvar svijeh namijenjenijeh smrti.
9 Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
Otvoraj usta svoja, sudi pravo, daj pravicu nevoljnome i ubogome.
10 Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
Ko æe naæi vrsnu ženu? jer vrijedi više nego biser.
11 Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
Oslanja se na nju srce muža njezina, i dobitka neæe nedostajati.
12 Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
Èini mu dobro, a ne zlo, svega vijeka svojega.
13 Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
Traži vune i lana, i radi po volji rukama svojim.
14 Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
Ona je kao laða trgovaèka, iz daleka donosi hranu svoju.
15 Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
Ustaje dok je još noæ, daje hranu èeljadi svojoj i posao djevojkama svojim.
16 Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
Misli o njivi, i uzme je, od rada ruku svojih sadi vinograd.
17 Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
Opasuje snagom bedra svoja i krijepi mišice svoje.
18 Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
Vidi kako joj je dobra radnja, ne gasi joj se noæu žižak.
19 Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
Rukama svojima maša se preslice, i prstima svojima drži vreteno.
20 Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
Ruku svoju otvora siromahu, i pruža ruke ubogome.
21 Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
Ne boji se snijega za svoju èeljad, jer sva èeljad njezina ima po dvoje haljine.
22 Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
Pokrivaèe sama sebi gradi, tako platno i skerlet odijelo joj je.
23 Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
Zna se muž njezin na vratima kad sjedi sa starješinama zemaljskim.
24 Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
Košulje gradi i prodaje, i pojase daje trgovcu.
25 Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
Odijelo joj je krjepost i ljepota, i osmijeva se na vrijeme koje ide.
26 Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
Usta svoja otvora mudro i na jeziku joj je nauka blaga.
27 Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
Pazi na vladanje èeljadi svoje, i hljeba u lijenosti ne jede.
28 Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
Sinovi njezini podižu se i blagosiljaju je; muž njezin takoðer hvali je;
29 “Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
Mnoge su žene bile vrsne, ali ti ih nadvišuješ sve.
30 Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
Ljupkost je prijevarna i ljepota tašta; žena koja se boji Gospoda, ona zaslužuje pohvalu.
31 Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.
Podajte joj od ploda ruku njezinijeh, i neka je hvale na vratima djela njezina.

< Miyambo 31 >