< Miyambo 30 >

1 Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
These things says the man to them that trust in God; and I cease.
2 “Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
For I am the most simple of all men, and there is not in me the wisdom of men.
3 Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
God has taught me wisdom, and I know the knowledge of the holy.
4 Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
Who has gone up to heaven, and come down? who has gathered the winds in his bosom? who has wrapped up the waters in a garment? who has dominion of all the ends of the earth? what is his name? or what is the name of his children?
5 “Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
For all the words of God are tried in the fire, and he defends those that reverence him.
6 Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
Add not to his words, lest he reprove you, and you be made a liar.
7 “Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
Two things I ask of you; take not favour from me before I die.
8 Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
Remove far from me vanity and falsehood: and give me not wealth [or] poverty; but appoint me what is needful and sufficient:
9 kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
lest I be filled and become false, and say, Who sees me? or be poor and steal, and swear [vainly] by the name of God.
10 “Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
Deliver not a servant into the hands of his master, lest he curse you, and you be utterly destroyed.
11 “Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
A wicked generation curse their father, and do not bless their mother.
12 Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
A wicked generation judge themselves to be just, but do not cleanse their way.
13 Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
A wicked generation have lofty eyes, and exalt themselves with their eyelids.
14 Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
A wicked generation have swords [for] teeth and jaw teeth [as] knives, so as to destroy and devour the lowly from the earth, and the poor of them from amongst men.
15 “Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
The horse-leech had three dearly beloved daughters: and these three did not satisfy her; and the fourth was not contented so as to say, Enough.
16 Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
The grave, and the love of a woman, and the earth not filled with water; water also and fire will not say, It is enough. (Sheol h7585)
17 Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
The eye that laughs to scorn a father, and dishonours the old age of a mother, let the ravens of the valleys pick it out, and let the young eagles devour it.
18 Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
Moreover there are three things impossible for me to comprehend, and the fourth I know not:
19 Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
the track of a flying eagle; and the ways of a serpent on a rock; and the paths of a ship passing through the sea; and the ways of a man in youth.
20 Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
Such is the way of an adulterous woman, who having washed herself from what she has done, says she has done nothing amiss.
21 Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
By three thing the earth is troubled, and the fourth it can’t bear:
22 Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
if a servant reign; or a fool be filled with food;
23 mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
or if a maidservant should cast out her own mistress; and if a hateful woman should marry a good man.
24 Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
And [there are] four very little things upon the earth, but these are wiser than the wise:
25 Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
the ants which are weak, and [yet] prepare [their] food in summer;
26 mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
the rabbits also [are] a feeble race, who make their houses in the rocks.
27 dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
The locusts have no king, and [yet] march orderly at one command.
28 Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
And the eft, which supports itself by [its] hands, and is easily taken, dwells in the fortresses of kings.
29 “Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
And there are three things which go well, and a fourth which passes along finely.
30 Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
A lion's whelp, stronger than [all other] beasts, which turns not away, nor fears [any] beast;
31 Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
and a cock walking in boldly amongst the hens, and the goat leading the herd; and a king publicly speaking before a nation.
32 “Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
If you abandon yourself to mirth, and stretch forth your hand in a quarrel, you shall be disgraced.
33 Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”
Milk out milk, and there shall be butter, and if you wing [one's] nostrils there shall come out blood: so if you extort words, there will come forth quarrels and strifes.

< Miyambo 30 >