< Miyambo 29 >

1 Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
Èovjek koji po karanju ostaje tvrdoglav, ujedanput æe propasti, da neæe biti lijeka.
2 Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
Kad se umnožavaju pravednici, veseli se narod; a kad vlada bezbožnik, uzdiše narod.
3 Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
Ko ljubi mudrost, veseli oca svojega; a ko se druži s kurvama, rasipa svoje dobro.
4 Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
Car pravdom podiže zemlju; a ko uzima mito, satire je.
5 Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
Ko laska prijatelju svojemu, razapinje mrežu nogama njegovijem.
6 Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
U grijehu je zla èovjeka zamka, a pravednik pjeva i veseli se.
7 Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
Pravednik razumije parbu nevoljnijeh, a bezbožnik ne mari da zna.
8 Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
Potsmjevaèi raspaljuju grad, a mudri utišavaju gnjev.
9 Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
Mudar èovjek kad se pre s ludijem, ili se srdio ili smijao, nema mira.
10 Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
Krvopije mrze na bezazlenoga, a pravi se brinu za dušu njegovu.
11 Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
Sav gnjev svoj izliva bezumnik, a mudri ustavlja ga natrag.
12 Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
Koji knez sluša lažne rijeèi, sve su mu sluge bezbožne.
13 Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
Siromah i koji daje na dobit sretaju se; obojici Gospod prosvjetljuje oèi.
14 Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
Koji car pravo sudi siromasima, njegov æe prijesto stajati dovijeka.
15 Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
Prut i kar daju mudrost, a dijete pusto sramoti mater svoju.
16 Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
Kad se umnožavaju bezbožnici, umnožavaju se grijesi, a pravednici æe vidjeti propast njihovu.
17 Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
Karaj sina svojega, i smiriæe te, i uèiniæe milinu duši tvojoj.
18 Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
Kad nema utvare, rasipa se narod; a ko drži zakon, blago njemu!
19 Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
Rijeèima se ne popravlja sluga, jer ako i razumije, opet ne sluša.
20 Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
Jesi li vidio èovjeka nagla u besjedi svojoj? više ima nadanja od bezumna nego od njega.
21 Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
Ako ko mazi slugu od malena, on æe najposlije biti sin.
22 Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
Gnjevljiv èovjek zameæe svaðu, i ko je naprasit, mnogo griješi.
23 Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
Oholost ponižuje èovjeka, a ko je smjeran duhom, dobija slavu.
24 Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
Ko dijeli s lupežem, mrzi na svoju dušu, èuje prokletstvo i ne prokazuje.
25 Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
Strašiv èovjek meæe sebi zamku; a ko se u Gospoda uzda, biæe u visokom zaklonu.
26 Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
Mnogi traže lice vladaoèevo, ali je od Gospoda sud svakome.
27 Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.
Pravednima je mrzak nepravednik, a bezbožniku je mrzak ko pravo hodi.

< Miyambo 29 >