< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Kad sjedeš da jedeš s gospodinom, pazi dobro što je pred tobom.
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
Inaèe bi satjerao sebi nož u grlo, ako bi bio lakom.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Ne želi preslaèaka njegovijeh, jer su lažna hrana.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Ne muèi se da se obogatiš, i proði se svoje mudrosti.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Hoæeš li baciti oèi svoje na ono èega brzo nestaje? jer naèini sebi krila i kao orao odleti u nebo.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Ne jedi hljeba u zavidljivca, i ne želi preslaèaka njegovijeh.
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
Jer kako on tebe cijeni u duši svojoj tako ti jelo njegovo. Govoriæe ti: jedi i pij; ali srce njegovo nije s tobom.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Zalogaj što pojedeš izbljuvaæeš, i izgubiæeš ljubazne rijeèi svoje.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Pred bezumnijem ne govori, jer neæe mariti za mudrost besjede tvoje.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Ne pomièi stare meðe, i ne stupaj na njivu siroèadi.
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
Jer je jak osvetnik njihov; braniæe stvar njihovu od tebe.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Obrati k nauci srce svoje i uši svoje k rijeèima mudrijem.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Ne ukraæuj kara djetetu; kad ga biješ prutom, neæe umrijeti.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Ti ga bij prutom, i dušu æeš mu izbaviti iz pakla. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Sine moj, ako bude mudro srce tvoje, veseliæe se srce moje u meni;
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
I igraæe bubrezi moji kad usne tvoje stanu govoriti što je pravo.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Srce tvoje neka ne zavidi grješnicima, nego budi u strahu Gospodnjem vazda.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
Jer ima plata, i nadanje tvoje neæe se zatrti.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Slušaj, sine moj, i budi mudar i upravi putem srce svoje.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Ne budi meðu pijanicama ni meðu izjelicama.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
Jer pijanica i izjelica osiromašiæe, i spavaè hodiæe u ritama.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Slušaj oca svojega koji te je rodio, i ne preziri matere svoje kad ostari.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Kupuj istinu i ne prodaji je; kupuj mudrost, znanje i razum.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Veoma se raduje otac pravednikov, i roditelj mudroga veseli se s njega.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Neka se dakle veseli otac tvoj i mati tvoja, i neka se raduje roditeljka tvoja.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Sine moj, daj mi srce svoje, i oèi tvoje neka paze na moje pute.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Jer je kurva duboka jama, a tijesan studenac tuða žena.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Ona i zasjeda kao lupež i umnožava zloèince meðu ljudima.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
Kome: jaoh? kome: kuku? kome svaða? kome vika? kome rane ni za što? kome crven u oèima?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Koji sjede kod vina, koji idu te traže rastvorena vina.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Ne gledaj na vino kad se rumeni, kad u èaši pokazuje lice svoje i upravo iskaèe.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
Na pošljedak æe kao zmija ujesti i kao aspida upeæi.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Oèi æe tvoje gledati na tuðe žene, i srce æe tvoje govoriti opaèine.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
I biæeš kao onaj koji leži usred mora i kao onaj koji spava navrh jedra.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
Reæi æeš: izbiše me, ali me ne zabolje; tukoše me, ali ne osjetih; kad se probudim, iæi æu opet da tražim to.

< Miyambo 23 >