< Miyambo 23 >

1 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
Gdy usiądziesz do posiłku z władcą, zważaj pilnie, co jest przed tobą;
2 ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
I przyłóż nóż do gardła, jeśli jesteś łakomy.
3 Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
Nie pragnij jego przysmaków, bo to pokarm zwodniczy.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
Nie zabiegaj o bogactwo, porzuć swoją mądrość.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
Czy obrócisz swoje oczy na to, co jest niczym? Bo bogactwa robią sobie skrzydła i ulatują do nieba jak orzeł.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
Nie jedz chleba człowieka, który ma złe oko, ani nie pożądaj jego przysmaków.
7 paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
Bo jak myśli w swym sercu, taki [on jest]. Jedz i pij – mówi do ciebie, ale jego serce nie jest z tobą.
8 Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
Kęs, który zjadłeś, zwrócisz i utracisz swoje wdzięczne słowa.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
Nie mów do uszu głupca, bo wzgardzi mądrością twoich słów.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
Nie przesuwaj dawnej granicy i nie wchodź na pole sierot.
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
Bo ich obrońca jest mocny, przeprowadzi ich sprawę przeciwko tobie.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
Nakłoń swoje serce na pouczenie, a swe uszy na słowa rozumne.
13 Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
Nie szczędź dziecku karcenia, [bo] jeśli je bijesz rózgą, nie umrze.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
Będziesz je bił rózgą, a jego duszę ocalisz od piekła. (Sheol h7585)
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
Synu mój, jeśli twoje serce będzie mądre, moje serce będzie się radowało, właśnie moje;
16 Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
I moje nerki będą się weselić, gdy twoje usta będą mówiły to, co jest prawe.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
Niech twoje serce nie zazdrości grzesznikom, lecz każdego dnia [postępuj] w bojaźni PANA;
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
Bo koniec jest pewny i twoja nadzieja nie będzie zawiedziona.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
Słuchaj, synu mój, i bądź mądry, i skieruj swoje serce na drogę.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
Nie bywaj wśród pijaków ani wśród obżerających się mięsem;
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
Bo pijak i żarłok zubożeją, a ospały będzie chodził w łachmanach.
22 Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
Słuchaj ojca, który cię spłodził, a nie gardź matką, gdy się zestarzeje.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
Kupuj prawdę i nie sprzedawaj [jej]; [kupuj] mądrość, karność i rozum.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
Ojciec sprawiedliwego będzie się wielce radował, a kto spłodzi mądrego, będzie się z niego cieszył.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
Niech się weseli twój ojciec i matka i niech się raduje ta, która cię rodziła.
26 Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
Synu mój, daj mi swoje serce, a niech twoje oczy strzegą moich dróg.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
Bo nierządnica [jest] głębokim dołem, a cudza [kobieta jest] ciasną studnią.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
Ona też czyha jak zbój i pomnaża przewrotnych wśród ludzi.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
U kogo biada? U kogo żal? U kogo kłótnie? U kogo szemranie? Kto ma rany bez powodu? Kto ma zaczerwienione oczy?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
Ci, którzy przesiadują przy winie; ci, którzy idą szukać zmieszanego wina.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
Nie patrz na wino, gdy się czerwieni; gdy wydaje łunę swą w kielichu, a samo się przesuwa.
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
Na koniec ugryzie jak wąż i ukąsi jak żmija;
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
Twoje oczy będą patrzeć na cudze kobiety, a twoje serce będzie mówiło rzeczy przewrotne;
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
I będziesz jak ten, który leży na środku morza, i jak ten, który śpi na szczycie masztu;
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
[Powiesz]: Bili mnie, a nie bolało, uderzyli mnie, a [nic] nie czułem. Gdy się obudzę, znów go poszukam.

< Miyambo 23 >