< Miyambo 21 >

1 Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
Srce je carevo u ruci Gospodu kao potoci vodeni; kuda god hoæe, savija ga.
2 Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
Svaki se put èovjeku èini prav, ali Gospod ispituje srca.
3 Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
Da se èini pravda i sud, milije je Gospodu nego žrtva.
4 Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
Ponosite oèi i naduto srce i oranje bezbožnièko grijeh je.
5 Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
Misli vrijedna èovjeka donose obilje, a svakoga nagla siromaštvo.
6 Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
Blago sabrano jezikom lažljivijem taština je koja prolazi meðu one koji traže smrt.
7 Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
Grabež bezbožnijeh odnijeæe ih, jer ne htješe èiniti što je pravo.
8 Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
Èiji je put kriv, on je tuð; a ko je èist, njegovo je djelo pravo.
9 Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
Bolje je sjedjeti u uglu od krova nego sa ženom svadljivom u kuæi zajednièkoj.
10 Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
Duša bezbožnikova želi zlo, ni prijatelj njegov ne nalazi milosti u njega.
11 Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
Kad potsmjevaè biva karan, ludi mudra; i kad se mudri pouèava, prima znanje.
12 Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
Uèi se pravednik od kuæe bezbožnikove, kad se bezbožnici obaraju u zlo.
13 Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
Ko zatiskuje uho svoje od vike ubogoga, vikaæe i sam, ali neæe biti uslišen.
14 Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
Dar u tajnosti utišava gnjev, i poklon u njedrima žestoku srdnju.
15 Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
Radost je pravedniku èiniti što je pravo, a strah onima koji èine bezakonje.
16 Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
Èovjek koji zaðe s puta mudrosti poèinuæe u zboru mrtvijeh.
17 Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
Ko ljubi veselje, biæe siromah; ko ljubi vino i ulje, neæe se obogatiti.
18 Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
Otkup za pravednike biæe bezbožnik i za dobre bezakonik.
19 Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
Bolje je živjeti u zemlji pustoj nego sa ženom svadljivom i gnjevljivom.
20 Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
Dragocjeno je blago i ulje u stanu mudroga, a èovjek bezuman proždire ga.
21 Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
Ko ide za pravdom i milošæu, naæi æe život, pravdu i slavu.
22 Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
U grad jakih ulazi mudri, i obara silu u koju se uzdaju.
23 Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
Ko èuva usta svoja i jezik svoj, èuva dušu svoju od nevolja.
24 Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
Ponositom i obijesnom ime je potsmjevaè, koji sve radi bijesno i oholo.
25 Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
Ljenivca ubija želja, jer ruke njegove neæe da rade;
26 Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
Svaki dan želi; a pravednik daje i ne štedi.
27 Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
Žrtva je bezbožnièka gad, akamoli kad je prinose u grijehu?
28 Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
Lažni svjedok poginuæe, a èovjek koji sluša, govoriæe svagda.
29 Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
Bezbožnik je bezobrazan, a pravednik udešava svoje pute.
30 Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
Nema mudrosti ni razuma ni savjeta nasuprot Bogu.
31 Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.
Konj se oprema za dan boja, ali je u Gospoda spasenje.

< Miyambo 21 >