< Miyambo 19 >

1 Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
Siromah koji hodi u bezazlenosti svojoj bolji je nego opaki usnama svojim, koji je bezuman.
2 Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
Kad je duša bez znanja, nije dobro; i ko je brzijeh nogu, spotièe se.
3 Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
Ludost èovjeèija prevraæa put njegov, a srce se njegovo gnjevi na Gospoda.
4 Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
Bogatstvo pribavlja mnogo prijatelja, a siromaha ostavlja prijatelj njegov.
5 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
Lažan svjedok neæe ostati bez kara, i ko govori laž, neæe uteæi.
6 Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
Mnogi ugaðaju knezu, i svak je prijatelj èovjeku podatljivu.
7 Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
Na siromaha mrze sva braæa njegova, još više se prijatelji njegovi udaljuju od njega; vièe za njima, ali ih nema.
8 Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
Ko pribavlja razum, ljubi dušu svoju; i ko pazi na mudrost, naæi æe dobro.
9 Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
Svjedok lažan neæe ostati bez kara, i ko govori laž, poginuæe.
10 Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
Ne dolikuju bezumnom miline, ni sluzi da vlada knezovima.
11 Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
Razum zadržava èovjeka od gnjeva, i èast mu je mimoiæi krivicu.
12 Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
Careva je srdnja kao rika mladoga lava, i ljubav je njegova kao rosa travi.
13 Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
Bezuman je sin muka ocu svojemu, i svadljivost ženina neprestano prokisivanje.
14 Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
Kuæa i imanje našljeðuje se od otaca; a od Gospoda je razumna žena.
15 Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
Lijenost navodi tvrd san, i nemarljiva duša gladovaæe.
16 Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
Ko drži zapovijesti, èuva dušu svoju; a ko ne mari za putove svoje, poginuæe.
17 Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
Gospodu pozaima ko poklanja siromahu, i platiæe mu za dobro njegovo.
18 Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
Karaj sina svojega dokle ima nadanja, i na pogibao njegovu da ne prašta duša tvoja.
19 Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
Velik gnjev pokazuj kad praštaš kar, i kad oprostiš, poslije veæma pokaraj.
20 Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
Slušaj svjet i primaj nastavu, da poslije budeš mudar.
21 Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
Mnogo ima misli u srcu èovjeèijem, ali što Gospod naumi ono æe ostati.
22 Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
Želja èovjeku treba da je da èini milost, a bolji je siromah nego laža.
23 Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
Strah je Gospodnji na život; u koga je on, boravi sit, niti ga pohodi zlo.
24 Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
Ljenivac krije ruku svoju u njedra, ni k ustima svojim ne prinosi je.
25 Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
Udri potsmjevaèa da ludi omudra, i razumnoga nakaraj da razumije nauku.
26 Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
Sin sramotan i prijekoran upropašæuje oca i odgoni mater.
27 Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
Nemoj, sine, slušati nauke koja odvodi od rijeèi razumnijeh.
28 Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
Nevaljao svjedok potsmijeva se pravdi, i usta bezbožnièka proždiru nepravdu.
29 Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.
Gotovi su potsmjevaèima sudovi i bezumnicima boj na leða.

< Miyambo 19 >