< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Èovjek samovoljan traži što je njemu milo i miješa se u svašta.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
Bezumniku nije mio razum nego da se javlja srce njegovo.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Kad doðe bezbožnik, doðe i rug, i prijekor sa sramotom.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Rijeèi su iz usta èovjeèijih duboka voda, izvor je mudrosti potok koji se ražljeva.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Nije dobro gledati bezbožniku ko je, da se uèini krivo pravomu na sudu.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Usne bezumnikove pristaju u svaðu, i usta njegova dozivlju boj.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
Bezumniku su usta njegova pogibao, i usne njegove pruglo duši njegovoj.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Rijeèi su opadaèeve kao izbijenijeh, ali slaze unutra u trbuh.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
I ko je nemaran u poslu svom brat je raspikuæi.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Tvrda je kula ime Gospodnje, k njemu æe uteæi pravednik, i biæe u visokom zaklonu.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Bogatstvo je bogatome jak grad i kao visok zid u njegovoj misli.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Pred propast podiže se srce èovjeku, a prije slave ide smjernost.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Ko odgovara prije nego èuje, to mu je ludost i sramota.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
Duh èovjeèji snosi bol svoj; a duh oboren ko æe podignuti?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Srce razumna èovjeka dobavlja znanje, i uho mudrijeh traži znanje.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Dar èovjeku širi mjesto i vodi ga pred vlastelje.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Pravedan se èini ko je prvi u svojoj raspri, ali kad doðe bližnji njegov, ispituje se.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Raspre prekida ždrijeb, i izmeðu silnijeh rasuðuje.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Uvrijeðen je brat kao tvrd grad, i svaða je kao prijevornica na dvoru.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Svakomu se trbuh siti plodom usta njegovijeh, dohotkom od usana svojih siti se.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Smrt je i život u vlasti jeziku, i ko ga miluje, ješæe plod njegov.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Ko je našao ženu, našao je dobro i dobio ljubav od Gospoda.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Siromah govori moleæi, a bogat odgovara oštro.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
Ko ima prijatelja, valja da postupa prijateljski, jer ima prijatelja vjernijih od brata.

< Miyambo 18 >