< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
Samolub szuka tego, co mu się podoba, i wtrąca się w każdą sprawę.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
Głupi nie ma upodobania w rozumie, lecz w tym, co serce mu objawia.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
Gdy przychodzi niegodziwy, przychodzi też pogarda, a z hańbą urąganie.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Słowa ust człowieka są jak głębokie wody, a źródło mądrości jak płynący potok.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
Niedobrze przez wzgląd na osobę niegodziwą krzywdzić sprawiedliwego w sądzie.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
Wargi głupiego wchodzą w spór, a jego usta wołają o razy.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
Usta głupiego [są] jego zgubą, a jego wargi sidłem jego duszy.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
Słowa plotkarza są jak rany i przenikają do głębi wnętrzności.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
Kto jest niedbały w pracy, jest bratem marnotrawcy.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
Imię PANA [jest] potężną wieżą, sprawiedliwy ucieka do niej i jest bezpieczny.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
Zamożność bogacza [jest] jego warownym miastem i jak wysoki mur w jego wyobrażeniu.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
Przed upadkiem serce człowieka jest wyniosłe, a chwałę poprzedza pokora.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
Kto odpowiada, zanim wysłucha, [ujawnia] głupotę i [ściąga na] siebie hańbę.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
Duch człowieka zniesie jego chorobę, ale któż zniesie strapionego ducha?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
Serce rozumnego zdobywa wiedzę, a ucho mądrych szuka wiedzy.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
Dar człowieka toruje mu drogę i prowadzi go przed wielkich.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
Ten, który jest pierwszy w swojej sprawie, [zdaje się] sprawiedliwy, ale przychodzi jego bliźni i sprawdza go.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Los kładzie kres sporom i rozstrzyga między możnymi.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
Brat obrażony [trudniejszy do zdobycia] niż warowne miasto, a spory są jak rygle w zamku.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
Owocem swoich ust nasyci człowiek swoje wnętrze, nasyci się plonem swych warg.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Śmierć i życie są w mocy języka, a kto go miłuje, spożyje jego owoc.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
Kto znalazł żonę, znalazł coś dobrego i dostąpił łaski od PANA.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
Ubogi prosi pokornie, ale bogaty odpowiada surowo.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
Człowiek, który ma przyjaciół, musi obchodzić się z nimi po przyjacielsku, a jest przyjaciel, który przylgnie bardziej niż brat.

< Miyambo 18 >