< Miyambo 18 >

1 Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
He that wole go a wei fro a frend, sekith occasiouns; in al tyme he schal be dispisable.
2 Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
A fool resseyueth not the wordis of prudence; `no but thou seie tho thingis, that ben turned in his herte.
3 Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
A wickid man, whanne he cometh in to depthe of synnes, dispisith; but sclaundre and schenschipe sueth hym.
4 Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
Deep watir is the wordis of the mouth of a man; and a stronde fletinge ouer is the welle of wisdom.
5 Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
It is not good to take the persoone of a wickid man in doom, that thou bowe awei fro the treuthe of dom.
6 Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
The lippis of a fool medlen hem silf with chidyngis; and his mouth excitith stryues.
7 Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
The mouth of a fool is defoulyng of hym; and hise lippis ben the fallynge of his soule.
8 Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
The wordis of a double tungid man ben as symple; and tho comen `til to the ynnere thingis of the wombe. Drede castith doun a slowe man; forsothe the soulis of men turned in to wymmens condicioun schulen haue hungur.
9 Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
He that is neisch, and vnstidfast in his werk, is the brother of a man distriynge hise werkis.
10 Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
A strongeste tour is the name of the Lord; a iust man renneth to hym, and schal be enhaunsid.
11 Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
The catel of a riche man is the citee of his strengthe; and as a stronge wal cumpassinge hym.
12 Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
The herte of man is enhaunsid, bifor that it be brokun; and it is maad meke, bifore that it be glorified.
13 Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
He that answerith bifore that he herith, shewith hym silf to be a fool; and worthi of schenschipe.
14 Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
The spirit of a man susteyneth his feblenesse; but who may susteyne a spirit liyt to be wrooth?
15 Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
The herte of a prudent man schal holde stidfastli kunnyng; and the eere of wise men sekith techyng.
16 Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
The yift of a man alargith his weie; and makith space to hym bifore princes.
17 Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
A iust man is the first accusere of hym silf; his frend cometh, and schal serche hym.
18 Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
Lot ceessith ayenseiyngis; and demeth also among miyti men.
19 Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
A brother that is helpid of a brothir, is as a stidfast citee; and domes ben as the barris of citees.
20 Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
A mannus wombe schal be fillid of the fruit of his mouth; and the seedis of hise lippis schulen fille hym.
21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
Deth and lijf ben in the werkis of tunge; thei that louen it, schulen ete the fruytis therof.
22 Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
He that fyndith a good womman, fyndith a good thing; and of the Lord he schal drawe vp myrthe. He that puttith a wey a good womman, puttith awei a good thing; but he that holdith auowtresse, is a fool and vnwijs.
23 Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
A pore man schal speke with bisechingis; and a riche man schal speke sterneli.
24 Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.
A man freendli to felouschipe schal more be a frend, than a brothir.

< Miyambo 18 >