< Miyambo 14 >

1 Mkazi wanzeru amamanga banja lake, koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.
A wijs womman bildith hir hous; and an unwijs womman schal distrie with hondis an hous bildid.
2 Amene amayenda molungama amaopa Yehova, koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.
A man goynge in riytful weie, and dredinge God, is dispisid of hym, that goith in a weie of yuel fame.
3 Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana, koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.
The yerde of pride is in the mouth of a fool; the lippis of wijs men kepen hem.
4 Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya, koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.
Where oxis ben not, the cratche is void; but where ful many cornes apperen, there the strengthe of oxe is opyn.
5 Mboni yokhulupirika sinama, koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.
A feithful witnesse schal not lie; a gileful witnesse bringith forth a leesing.
6 Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza, koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.
A scornere sekith wisdom, and he fyndith not; the teching of prudent men is esy.
7 Khala kutali ndi munthu wopusa chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.
Go thou ayens a man a fool; and he schal not knowe the lippis of prudence.
8 Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake. Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.
The wisdom of a fel man is to vndirstonde his weie; and the vnwarnesse of foolis errith.
9 Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo, koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.
A fool scorneth synne; grace schal dwelle among iust men.
10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake, ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.
The herte that knowith the bittirnesse of his soule; a straunger schal not be meddlid in the ioie therof.
11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka, koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.
The hous of wickid men schal be don awei; the tabernaclis of iust men schulen buriowne.
12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu, koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.
Sotheli a weie is, that semeth iust to a man; but the laste thingis therof leden forth to deth.
13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa, ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.
Leiyyng schal be medlid with sorewe; and morenyng ocupieth the laste thingis of ioye.
14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake, koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.
A fool schal be fillid with hise weies; and a good man schal be aboue hym.
15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse, koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.
An innocent man bileueth to eche word; a felle man biholdith hise goyngis.
16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa, koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.
A wijs man dredith, and bowith awei fro yuel; a fool skippith ouer, and tristith.
17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru, ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.
A man vnpacient schal worche foli; and a gileful man is odiouse.
18 Anthu opusa amalandira uchitsiru, koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.
Litle men of wit schulen holde foli; and felle men schulen abide kunnyng.
19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino, ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.
Yuel men schulen ligge bifor goode men; and vnpitouse men bifor the yatis of iust men.
20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda, koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.
A pore man schal be hateful, yhe, to his neiybore; but many men ben frendis of riche men.
21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.
He that dispisith his neiybore, doith synne; but he that doith merci to a pore man, schal be blessid. He that bileueth in the Lord, loueth merci;
22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera? Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.
thei erren that worchen yuel. Merci and treuthe maken redi goodis;
23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu, koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.
abundaunce `schal be in ech good werk. Sotheli where ful many wordis ben, there nedynesse is ofte.
24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe, koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.
The coroun of wise men is the richessis of hem; the fooli of foolis is vnwarnesse.
25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo, koma mboni yabodza imaphetsa.
A feithful witnesse delyuereth soulis; and a fals man bringith forth leesyngis.
26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.
In the drede of the Lord is triste of strengthe; and hope schal be to the sones of it.
27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo, kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.
The drede of the Lord is a welle of lijf; that it bowe awei fro the fallyng of deth.
28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu, koma popanda anthu kalonga amawonongeka.
The dignite of the king is in the multitude of puple; and the schenschipe of a prince is in the fewnesse of puple.
29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri, koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.
He that is pacient, is gouerned bi myche wisdom; but he that is vnpacient, enhaunsith his foli.
30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo, koma nsanje imawoletsa mafupa.
Helthe of herte is the lijf of fleischis; enuye is rot of boonys.
31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake, koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.
He that falsli chalengith a nedi man, dispisith his maker; but he that hath merci on a pore man, onourith that makere.
32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe, koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.
A wickid man is put out for his malice; but a iust man hopith in his deth.
33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu, koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.
Wisdom restith in the herte of a wijs man; and he schal teche alle vnlerned men.
34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu, koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.
Riytfulnesse reisith a folc; synne makith puplis wretchis.
35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru, koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.
A mynystre vndurstondynge is acceptable to a kyng; a mynystre vnprofitable schal suffre the wrathfulnesse of him.

< Miyambo 14 >