< Miyambo 10 >

1 Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
Mudar je sin radost ocu svojemu, a lud je sin žalost materi svojoj.
2 Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
Ne pomaže nepravedno blago, nego pravda izbavlja od smrti.
3 Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
Ne da Gospod da gladuje duša pravednikova, a imanje bezbožnièko razmeæe.
4 Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
Nemarna ruka osiromašava, a vrijedna ruka obogaæava.
5 Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
Ko zbira u ljeto, sin je razuman; ko spava o žetvi, sin je sramotan.
6 Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
Blagoslovi su nad glavom pravedniku, a usta bezbožnièka pokriva nasilje.
7 Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
Spomen pravednikov ostaje blagosloven, a ime bezbožnièko truhne.
8 Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
Ko je mudra srca, prima zapovijesti; a ko je ludijeh usana, pašæe.
9 Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
Ko hodi bezazleno, hodi pouzdano; a ko je opak na putovima svojim, poznaæe se.
10 Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
Ko namiguje okom, daje muku; i ko je ludijeh usana, pašæe.
11 Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
Usta su pravednikova izvor životu, a usta bezbožnièka pokriva nasilje.
12 Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
Mrzost zameæe svaðe, a ljubav prikriva sve prijestupe.
13 Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
Na usnama razumnoga nalazi se mudrost, a za leða je bezumnoga batina.
14 Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
Mudri sklanjaju znanje, a usta ludoga blizu su pogibli.
15 Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
Bogatstvo je bogatima tvrd grad, siromaštvo je siromasima pogibao.
16 Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
Rad je pravednikov na život, dobitak bezbožnikov na grijeh.
17 Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
Ko prima nastavu, na putu je k životu; a ko odbacuje kar, luta.
18 Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
Ko pokriva mržnju, lažljivih je usana; i ko iznosi sramotu, bezuman je.
19 Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
U mnogim rijeèima ne biva bez grijeha; ali ko zadržava usne svoje, razuman je.
20 Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
Jezik je pravednikov srebro odabrano; srce bezbožnièko ne vrijedi ništa.
21 Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
Usne pravednikove pasu mnoge, a bezumni umiru s bezumlja.
22 Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
Blagoslov Gospodnji obogaæava a bez muke.
23 Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
Bezumniku je šala èiniti zlo, a razuman èovjek drži se mudrosti.
24 Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
Èega se boji bezbožnik, ono æe ga snaæi; a što pravednici žele, Bog æe im dati.
25 Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
Kao što prolazi oluja, tako bezbožnika nestaje; a pravednik je na vjeèitom temelju.
26 Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
Kakav je ocat zubima i dim oèima, taki je ljenivac onima koji ga šalju.
27 Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
Strah Gospodnji dodaje dane, a bezbožnicima se godine prekraæuju.
28 Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
Èekanje pravednijeh radost je, a nadanje bezbožnijeh propada.
29 Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
Put je Gospodnji krjepost bezazlenomu, a strah onima koji èine bezakonje.
30 Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
Pravednik se neæe nigda pokolebati, a bezbožnici neæe nastavati na zemlji.
31 Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
Usta pravednikova iznose mudrost, a jezik opaki istrijebiæe se.
32 Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.
Usne pravednikove znaju što je milo, a bezbožnièka su usta opaèina.

< Miyambo 10 >