< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Przysłowia Salomona, syna Dawida, króla Izraela;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Do poznania mądrości i karności, do zrozumienia słów roztropnych;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Do zdobycia pouczenia w mądrości, w sprawiedliwości, w sądzie i w prawości;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Do udzielenia prostym rozwagi, a młodemu – wiedzy i roztropności.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Mądry posłucha i przybędzie mu wiedzy, a rozumny nabędzie rad;
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Aby rozumieć przysłowia i [ich] wykładnię, słowa mądrych i ich zagadki.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Bojaźń PANA jest początkiem wiedzy, ale głupcy gardzą mądrością i karnością.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Synu mój, słuchaj pouczenia swego ojca i nie odrzucaj nauki swojej matki;
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Bo one będą wdzięczną ozdobą na twojej głowie i [kosztownym] łańcuchem na szyi.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Synu mój, jeśli grzesznicy cię namawiają, nie pozwalaj.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Jeśli mówią: Chodź z nami, czyhajmy na krew, zaczajmy się na niewinnego bez powodu;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Pożremy ich żywcem jak grób, całych, jak zstępujących do dołu; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Znajdziemy wszelkie kosztowności, napełnimy swoje domy łupem;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Dziel z nami swój los; miejmy wszyscy jedną sakiewkę.
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Synu mój, nie wyruszaj z nimi w drogę; powstrzymaj swoją nogę od ich ścieżki.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Ich nogi bowiem biegną do zła i spieszą się do przelania krwi.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Na próżno zastawia się sieci na oczach wszelkiego ptactwa.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Oni też czyhają na własną krew, czają się na własne życie.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Takie są ścieżki każdego, który jest chciwy zysku; swojemu właścicielowi [taki zysk] odbiera życie.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Mądrość woła na dworze, podnosi swój głos na ulicach.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
Woła w największym zgiełku, u wrót bram, w mieście wygłasza swoje słowa:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Jak długo, prości, będziecie kochać głupotę, szydercy – lubować się w swoim szyderstwie, a głupi – nienawidzić wiedzy?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Nawróćcie się na moje upomnienie; oto wyleję na was mojego ducha, oznajmię wam moje słowa.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Ponieważ wołałam, a odmawialiście; wyciągałam rękę, a nikt nie zważał;
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Owszem, odrzuciliście całą moją radę i nie chcieliście [przyjąć] mojego upomnienia;
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Dlatego będę się śmiać z waszego nieszczęścia, będę szydzić z was, gdy przyjdzie to, czego się boicie.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Gdy nadejdzie jak spustoszenie to, czego się boicie, i [gdy] wasze nieszczęście nadciągnie jak wicher, gdy nadejdzie na was ucisk i cierpienie;
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Wtedy będą mnie wzywać, a nie wysłucham; będą mnie szukać pilnie, lecz mnie nie znajdą.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Bo znienawidzili wiedzę i nie wybrali bojaźni PANA;
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ani nie chcieli mojej rady, [ale] gardzili każdym moim upomnieniem.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Dlatego spożyją owoc swoich dróg i będą nasyceni swymi radami.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Bo odstępstwo prostych zabije ich i szczęście głupich zgubi ich.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
[Ale] kto mnie słucha, będzie mieszkać bezpiecznie i będzie wolny od strachu przed złem.

< Miyambo 1 >