< Filemoni 1 >

1 Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
To my beloved friend and coworker Philemon,
2 Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
to my sister Apphia, to my fellow soldier Archippus, and to the church which meets at Philemon’s house. From Paul, a prisoner of Jesus Christ, and brother Timothy.
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Grace and peace be to you from God our Father and the Lord Jesus Christ.
4 Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
I am ever mentioning you in my prayers, and giving thanks to God,
5 Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
because I am hearing of your love and of the faith which you hold, not only toward the Lord Jesus Christ, but toward all the saints.
6 Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
And I pray that your participation may become effectual, as you come to acknowledge every good thing which is in you to Christ.
7 Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
For I have great joy and comfort in your love, my brother, because the hearts of the saints have been refreshed.
8 Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
And so, although I might be bold in Christ to dictate to you what is fitting,
9 komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
yet for love’s sake, I rather beseech you, I, Paul, an old man, and now a prisoner for Christ Jesus!
10 ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
I beseech you for my son, Onesimus, whom I have begotten in these chains.
11 Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
Once you found him "unprofitable," but now he is "profitable" to you and to me.
12 Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
I am sending him back to you, he himself, that is, my very heart!
13 Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
I could wish to retain him at my side, so that he might minister to me in your stead, in my bonds for the gospel.
14 Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
But without your consent I was unwilling to do anything, so that your kindness to me might be of your own free will, and not of compulsion.
15 Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios g166)
Perhaps for this reason you were separated from him for an hour, in order that you might have him back forever, (aiōnios g166)
16 Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
no longer as a slave, but more than a slave, as a brother beloved; especially dear to me, but how much more to you, both as a man and a fellow Christian.
17 Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
If then you count me as a partner, receive him as you would me.
18 Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
And if he has wronged you at all, or is owing you anything, charge that to me.
19 Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
I Paul am writing this in my own handwriting, "I will repay you." But I will not mention that you owe me, over and over, your very soul.
20 Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
Come my brother, let me have joy in the Lord because of you! Refresh my heart in Christ!
21 Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
Because I am thoroughly persuaded of your obedience, I have written you, knowing full well that you will do by me what I am asking.
22 Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
Please also prepare for me a lodging, for I am hoping by your prayers to be restored to you again.
23 Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
Epaphras, my fellow prisoner in Christ Jesus, sends you greeting;
24 Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
so do Mark, Aristarchus, Demas, and Luke, my fellow workers.
25 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.
May the grace of our Lord Jesus Christ be with your spirit. Amen.

< Filemoni 1 >