< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
I onaj dan kad Mojsije svrši i podiže šator, i kad ga pomaza i osveti sa svijem posuðem njegovijem i oltar sa svijem posuðem njegovijem, kad pomaza i osveti,
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Donesoše knezovi Izrailjevi, starješine u domovima otaca svojih, knezovi nad plemenima i poglavari od onijeh koji biše izbrojeni,
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
Donesoše prilog svoj pred Gospoda, šestora kola pokrivena i dvanaest volova, jedna kola dva kneza i po jednoga vola svaki, i donesoše pred šator.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
A Gospod reèe Mojsiju govoreæi:
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Uzmi to od njih da bude za službu u šatoru od sastanka, i podaj Levitima, svakomu prema službi njegovoj.
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
I uze Mojsije kola i volove, i dade ih Levitima.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Dvoja kola i èetiri vola dade sinovima Girsonovijem prema službi njihovoj.
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
A ostala èetvora kola i osam volova dade sinovima Merarijevim prema službi njihovoj pod upravom Itamara sina Arona sveštenika.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
A sinovima Katovijem ne dade ništa, jer im posao bijaše služiti svetinji, i nošahu na ramenima.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
I donesoše knezovi da se posveti oltar kad bi pomazan, donesoše knezovi priloge svoje pred oltar.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
A Gospod reèe Mojsiju: jedan knez u jedan dan a drugi knez u drugi dan neka donose svoje priloge da se posveti oltar.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
I prvi dan donese prilog svoj Nason sin Aminadavov od plemena Judina;
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
A prilog njegov bješe jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom; a oboje puno brašna bijeloga pomiješana s uljem za dar;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala, puna kada;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
Jedan jarac za grijeh;
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Nasona sina Aminadavova.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
Drugi dan donese Natanailo sin Sogarov, knez plemena Isaharova,
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
Donese prilog svoj: jednu zdjelu srebrnu od sto i trideset sikala, jednu èašu srebrnu od sedamdeset sikala po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
Jednu kadionicu zlatnu od deset sikala punu kada;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
Jedno tele, jednoga ovna, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
Jednoga jarca za grijeh;
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Natanaila sina Sogarova.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
Treæi dan donese knez sinova Zavulonovijeh, Elijav sin Helonov;
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
Njegov prilog bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, a oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Elijava sina Helonova.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
Èetvrti dan donese knez sinova Ruvimovijeh Elisur sin Sedijurov;
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Elisura sina Sedijurova.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
Peti dan donese knez sinova Simeunovijeh Salamilo sin Surisadajev;
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Salamila sina Surisadajeva.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
Šesti dan donese knez sinova Gadovijeh Elisaf sin Raguilov;
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Elisafa sina Raguilova.
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
Sedmi dan donese knez sinova Jefremovijeh Elisama sin Emijudov;
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Elisame sina Emijudova.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
Osmi dan donese knez sinova Manasijinih Gamalilo sin Fadasurov;
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Gamalila sina Fadasurova.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
Deveti dan donese knez sinova Venijaminovih Avidan sin Gadeonijev;
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Avidana sina Gadeonijeva.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
Deseti dan donese knez sinova Danovijeh Ahijezer sin Amisadajev;
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Ahijezera sina Amisadajeva.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
Jedanaesti dan donese knez sinova Asirovijeh Fagailo sin Ehranov;
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Fagaila sina Ehranova.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
Dvanaesti dan donese knez sinova Neftalimovijeh Ahirej sin Enanov;
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
Prilog njegov bješe: jedna zdjela srebrna od sto i trideset sikala, jedna èaša srebrna od sedamdeset sikala, po siklu svetom, oboje puno bijeloga brašna pomiješana s uljem za dar;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
Jedna kadionica zlatna od deset sikala puna kada;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
Jedno tele, jedan ovan, jedno jagnje od godine za žrtvu paljenicu;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
Jedan jarac za grijeh;
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
A za žrtvu zahvalnu dva vola, pet ovnova, pet jaraca, pet jaganjaca od godine. To bi prilog Ahireja sina Enanova.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
To je prilog od knezova Izrailjevijeh da se posveti oltar pošto bi pomazan: dvanaest zdjela srebrnijeh, dvanaest èaša srebrnijeh, dvanaest kadionica zlatnijeh;
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
Svaka zdjela srebrna od sto i trideset sikala, i svaka èaša od sedamdeset sikala; svega srebra u tijem sudovima dvije tisuæe i èetiri stotine sikala, po siklu svetom;
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
Dvanaest kadionica zlatnijeh punijeh kada, svaka kadionica od deset sikala, po siklu svetom; svega zlata u kadionicama sto i dvadeset sikala;
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
Svega stoke za žrtvu paljenicu dvanaest telaca, dvanaest ovnova, dvanaest jaganjaca od godine s darom svojim, i jaraca dvanaest za grijeh;
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
A svega stoke za žrtvu zahvalnu dvadeset i èetiri vola, šezdeset ovnova, šezdeset jaraca, šezdeset jaganjaca od godine. To bi prilog da se posveti oltar, pošto bi pomazan.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
I kad Mojsije ulažaše u šator od sastanka da govori pred Bogom, tada èujaše glas gdje mu govori sa zaklopca što bješe na kovèegu od svjedoèanstva izmeðu dva heruvima; i govoraše mu.

< Numeri 7 >