< Numeri 5 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
Zapovjedi sinovima Izrailjevijem neka istjeraju iz okola sve gubave i sve kojima teèe sjeme i sve koji su se oskvrnili o mrtvaca,
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
Bio èovjek ili žena, istjerajte, iza okola istjerajte ih, da ne skvrne okola onima meðu kojima nastavam.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
I uèiniše tako sinovi Izrailjevi, i istjeraše ih iz okola; kako Gospod kaza Mojsiju, tako uèiniše sinovi Izrailjevi.
5 Yehova anati kwa Mose,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
Reci sinovima Izrailjevijem: èovjek ili žena kad uèini kakav grijeh ljudski, te zgriješi Gospodu, i bude ona duša kriva,
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
Tada neka priznadu grijeh koji su uèinili, i ko je kriv neka vrati cijelo èim je kriv i neka dometne ozgo peti dio i da onomu kome je skrivio.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
I ako onaj nema nikoga komu bi pripala naknada za štetu, neka se da Gospodu i neka bude svešteniku osim ovna za oèišæenje kojim æe ga oèistiti.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
Tako i svaki prinos izmeðu svijeh stvari koje posveæuju sinovi Izrailjevi i donose svešteniku, njegov neka bude;
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
I što god ko posveti, neka je njegovo, i što god ko da svešteniku, neka je njegovo.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
Kaži sinovima Izrailjevim i reci im: èija bi žena zastranila te bi mu zgriješila,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
I drugi bi je obležao, a muž njezin ne bi znao, nego bi ona zatajila da se oskvrnila, i ne bi bilo svjedoka na nju, niti bi se zatekla,
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
A njemu bi došla sumnja ljubavna, te bi iz ljubavi sumnjao na svoju ženu, a ona bi bila oskvrnjena; ili bi mu došla sumnja ljubavna te bi iz ljubavi sumnjao na svoju ženu, a ona ne bi bila oskvrnjena;
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
Onda neka muž dovede ženu svoju k svešteniku, i neka donese za nju prinos njezin, deseti dio efe brašna jeèmenoga, ali neka ga ne polije uljem i neka ne metne na nj kada, jer je prinos za sumnju ljubavnu, dar za spomen da se spomene grijeh;
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
I neka je sveštenik privede i postavi pred Gospodom.
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
I neka uzme sveštenik svete vode u sud zemljani; i praha s poda u šatoru neka uzme i uspe u vodu.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
I postavivši sveštenik ženu pred Gospodom neka joj otkrije glavu i metne joj na ruke dar za spomen koji je dar za sumnju ljubavnu; a sveštenik neka drži u ruci svojoj gorku vodu, koja nosi prokletstvo.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
I neka sveštenik zakune ženu, i reèe joj: ako nije niko spavao s tobom, i ako nijesi zastranila od muža svojega na neèistotu, neka ti ne bude ništa od ove vode gorke, koja nosi prokletstvo.
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
Ako li si zastranila od muža svojega i oskvrnila se, i kogod drugi osim muža tvojega spavao s tobom,
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
Tada sveštenik zaklinjuæi ženu neka je prokune i reèe ženi: da te Gospod postavi za uklin i za kletvu u narodu tvom uèinivši da ti bedro spadne a trbuh oteèe.
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
I neka ti ova voda prokleta uðe u crijeva da ti oteèe trbuh i da ti bedro spadne. A žena neka reèe: amin, amin.
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
Tada neka napiše sveštenik te kletve u knjigu, i neka ih spere vodom gorkom.
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
I neka da ženi da se napije gorke vode proklete da uðe u nju voda prokleta i bude gorka.
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
I neka uzme sveštenik iz ruku ženi dar za sumnju ljubavnu, i obrne dar pred Gospodom i prinese ga na oltaru.
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
I neka uzme sveštenik u šaku od dara njezina spomen, i zapali na oltaru, pa onda neka da ženi vodu da popije.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
A kad joj da vodu da pije, ako se bude oskvrnila i uèinila nevjeru mužu svojemu, onda æe uæi voda prokleta u nju i postaæe gorka, i trbuh æe joj oteæi i spasti bedro, i ona æe žena postati uklin u narodu svojem.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
Ako li se ne bude oskvrnila žena, nego bude èista, neæe joj biti ništa i imaæe djece.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
Ovo je zakon za sumnju ljubavnu, kad žena zastrani od muža svojega i oskvrni se;
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
Ili kad kome doðe sumnja ljubavna te posumnja iz ljubavi na ženu svoju i postavi je pred Gospodom i svrši joj sveštenik sve po ovom zakonu.
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
I muž da je prost od grijeha, ali žena da nosi svoje bezakonje.

< Numeri 5 >