< Numeri 35 >

1 Ku zigwa za Mowabu pafupi ndi Yorodani ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju u polju Moavskom na Jordanu prema Jerihonu govoreæi:
2 “Lamula Aisraeli kuti apereke kwa Alevi midzi yoti azikhalamo kuchokera pa cholowa chomwe adzalandira. Muwapatsenso malo oweteramo ziweto kuzungulira midziyo.
Zapovjedi sinovima Izrailjevijem neka dadu od našljedstva svojega Levitima gradove, gdje æe živjeti; i podgraða oko gradova podajte im,
3 Midziyo idzakhala yawo ndipo azidzakhala mʼmenemo. Malo a msipu adzakhala a ngʼombe, nkhosa ndi zoweta zawo zina zonse.
Da u gradovima žive, a u podgraðima njihovijem da im stoji stoka i imanje njihovo i sve životinje njihove.
4 “Malo a msipu a mudziwo amene mudzawapatse Aleviwo, adzayambire ku khoma la mudzi ndipo adzatuluke kunja mamita 450, kuzungulira mudziwo.
A podgraða koja date Levitima neka budu na tisuæu lakata daleko od zidova gradskih unaokolo.
5 Kunja kwa mudzi yezani mamita 900 kummawa, mamita 900 kumpoto ndipo mudziwo ukhale pakati. Adzakhala ndi dera limeneli ngati malo a midziyo, owetera ziweto zawo.
Zato izmjerite iza svakoga grada na istok dvije tisuæe lakata, i na jug dvije tisuæe lakata, i na zapad dvije tisuæe lakata, i na sjever dvije tisuæe lakata, tako da grad bude u srijedi. Tolika neka budu podgraða njihova.
6 “Isanu ndi umodzi mwa midzi imene mudzapereke kwa Alevi idzakhala mizinda yopulumukirako, kumene munthu wopha mnzake adzathawireko. Ndipo mudzawapatsenso midzi ina 42.
A od gradova koje date Levitima odvojte šest gradova za utoèište, da onamo uteèe ko bi koga ubio; i osim njih podajte im èetrdeset i dva grada.
7 Midzi yonse imene mudzapereke kwa Alevi idzakhale 48, pamodzi ndi malo oweterako ziweto.
Svega gradova, koje æete dati Levitima da bude èetrdeset i osam gradova, svaki sa svojim podgraðem.
8 Pamene mukupatula midzi imeneyi pa cholowa cha Aisraeli, muchotsepo midzi yambiri pa mafuko aakulu, ndipo midzi pangʼono pa mafuko aangʼono. Fuko lililonse lidzapereka kwa Alevi molingana ndi kukula kwa cholowa chimene lalandira.”
A tijeh gradova što æete dati od našljedstva sinova Izrailjevijeh, od onijeh koji imaju više podajte više, a od onijeh koji imaju manje podajte manje; svaki prema našljedstvu koje æe imati neka da od svojih gradova Levitima.
9 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Još reèe Gospod Mojsiju govoreæi:
10 “Yankhula ndi Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mu Kanaani,
Reci sinovima Izrailjevijem i kaži im: kad prijeðete preko Jordana u zemlju Hanansku,
11 sankhani midzi ina kuti ikhale mizinda yanu yopulumukirako, kumene munthu wopha munthu wina mwangozi angathawireko.
Od gradova koji vam dopadnu odvojte gradove za utoèište da u njih uteèe krvnik koji ubije koga nehotice.
12 Adzakhala malo obisalako pothawa munthu wofuna kulipsira, kuti munthu wopha mnzake mwangozi asaphedwe mpaka akayime pamaso pa gulu la anthu kuti akaweruzidwe.
I ti æe vam gradovi biti utoèišta od osvetnika, da ne pogine krvnik dokle ne stane na sud pred zbor.
13 Midzi isanu ndi umodzi imene muyiperekeyi idzakhala mizinda yopulumukirako.
I tako od tijeh gradova koje date šest gradova biæe vam utoèišta.
14 Mupereke itatu mbali ino ya Yorodani ndi itatu ina mu Kanaani kuti ikhale mizinda yopulumukirako.
Tri taka grada podajte s ovu stranu Jordana, a tri grada podajte u zemlji Hananskoj, ti gradovi neka budu utoèišta.
15 Midzi isanu ndi umodzi idzakhala malo opulumukirako Aisraeli, alendo ndi anthu ena onse okhala pakati pawo kuti wina aliyense wopha mnzake mwangozi adzathawireko.
Sinovima Izrailjevijem i došljaku i strancu, koji se bavi meðu njima, neka tijeh šest gradova budu utoèišta, da uteèe u njih ko god ubije koga nehotice.
16 “‘Ngati munthu amenya mnzake ndi chitsulo, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo aphedwe.
Ali ako gvožðem udari koga, te onaj umre, krvnik je, neka se pogubi taki krvnik.
17 Kapenanso ngati wina wake ali ndi mwala mʼdzanja mwake womwe ungaphe munthu, ndipo agenda nawo wina, munthu winayo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha ndipo wakuphayo adzayenera kuphedwa.
I ako kamenom iz ruke, od kojega može èovjek poginuti, udari koga, te onaj umre, krvnik je, neka se pogubi taki krvnik.
18 Kapenanso ngati wina ali ndi chibonga mʼdzanja mwake choti nʼkupha nacho munthu, namenya nacho munthu, munthuyo nʼkufa, ndiye kuti iyeyo ndi wakupha, wakuphayo ayenera kuphedwa.
Ili ako drvetom iz ruke, od kojega može èovjek poginuti, udari koga, te onaj umre, krvnik je, neka se pogubi taki krvnik.
19 Wolipsira adzamuphanso wakuphayo. Pamene akumana naye adzayenera kumupha ndithu.
Osvetnik neka pogubi krvnika; kad ga udesi, neka ga pogubi.
20 Ndipo ngati wina wake, chifukwa cha udani, aganiza zokankha munthu wina kapena kumuponyera chinthu china mwadala munthuyo nʼkufa,
Ako ga iz mržnje turi, ili se baci èim na nj navalice, te onaj umre,
21 kapena ngati, chifukwa cha udani, amenya mnzake ndi nkhonya, mnzakeyo ndi kufa, munthuyo ayenera kuphedwa. Iyeyo ndi wakupha. Wolipsira adzamuphe wakuphayo pamene akumana naye.
Ili ako ga iz neprijateljstva udari rukom, te onaj umre, neka se pogubi taki ubojica, krvnik je; osvetnik neka pogubi toga krvnika kad ga udesi.
22 “‘Koma ngati popanda udani wina uliwonse, mwadzidzidzi akankha wina kapena kumuponyera chinthu osati mwadala,
Ako li ga nehotice turi bez neprijateljstva, ili se baci na nj èim nehotice,
23 kapena mosamuona nʼkumuponyera mwala womwe utha kumupha, munthuyo nʼkufa, tsono pakuti sanali mdani wake ndipo sanaganizire zomupweteka,
Ili kamenom od kojega može èovjek poginuti, ako se baci na nj nehotice, te onaj umre, a nije mu neprijatelj, niti mu traži zla,
24 gulu liweruze pakati pa iye ndi wolipsira monga mwa malamulo ake.
Tada da sudi zbor izmeðu ubojice i osvetnika po ovom zakonu.
25 Gulu lidzapulumutsa munthu wakuphayo mʼmanja mwa wolipsira uja ndi kumubwezera ku mzinda wopulumukirako kumene anathawira. Ayenera kukhala kumeneko kufikira imfa ya mkulu wa ansembe, amene anadzozedwa ndi mafuta oyera.
I zbor neka izbavi krvnika iz ruke osvetnikove i vrati ga u utoèište njegovo, kuda je utekao, i ondje neka ostane dokle ne umre poglavar sveštenièki, koji je pomazan svetim uljem.
26 “‘Koma ngati wolakwayo atuluka kunja kwa malire a mzinda wopulumukirako kumene anathawira
Ako krvnik kako god izide preko meðe svojega utoèišta, u koje je utekao,
27 ndipo wobwezera choyipa nʼkumupeza kunja kwa mzindawo, wolipsirayo atha kumupha wolakwayo popanda kugamula mlandu wakupha.
I naðe ga osvetnik preko meðe utoèišta njegova, ako krvnika ubije osvetnik, neæe biti kriv za krv.
28 Wolakwayo ayenera kukhala mu mzinda wopulumukiramowo mpaka imfa ya mkulu wa ansembe ndipo pamenepo atha kubwerera kwawo. Pokhapokha atafa mkulu wa ansembe ndi pamene angathe kubwerera ku malo ake.
Jer u utoèištu svojem valja da stoji dokle ne umre poglavar sveštenièki; pa kad umre poglavar sveštenièki, onda treba da se vrati krvnik u zemlju našljedstva svojega.
29 “‘Amenewa akhale malamulo ndi malangizo kwa inu nthawi zonse ndi ku mibado ya mʼtsogolo, kulikonse kumene mudzakhalako.
Ovo da vam je uredba za suðenje od koljena do koljena po svijem stanovima vašim.
30 “‘Aliyense wopha munthu ayeneranso kuphedwa ngati pali umboni okwanira. Koma wina asaphedwe ngati pali mboni imodzi yokha.
Ko bi htio pogubiti èovjeka, po svjedocima neka pogubi krvnika; ali jedan svjedok ne može svjedoèiti da se ko pogubi.
31 “‘Osalola kulandira dipo lowombolera munthu wakupha yemwe ayenera kuphedwa. Wakupha ayenera kuphedwa.
Ne uzimajte otkupa za krvnika, koji zasluži smrt, nego neka se pogubi.
32 “‘Simuyeneranso kulandira dipo kwa munthu amene wathawira ku mzinda wopulumikirako kuti wothawayo abwerere kwawo, pokhapokha ngati mkulu wa ansembe wamwalira.
Ni od onoga ne uzimajte otkupa koji uteèe u utoèište, da bi se vratio da živi u svojoj zemlji prije nego umre sveštenik;
33 “‘Musayipitse dziko limene mukukhalamolo. Magazi amayipitsa dziko ndipo nʼkosatheka kulipirira dziko chifukwa cha magazi amene akhetsedwa mʼmenemo, kupatula pokhetsa magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.
Da ne biste skvrnili zemlju u kojoj ste, jer krv ona skvrni zemlju, a zemlja se ne može oèistiti od krvi koja se prolije na njoj drukèije nego krvlju onoga koji je prolije.
34 Choncho musadetse dziko limene mukukhalamo, dziko limene Inenso ndimakhalamo, pakuti Ine Yehova, ndimakhala pakati pa Aisraeli.’”
Zato ne skvrnite zemlje u kojoj nastavate i u kojoj ja nastavam, jer ja Gospod nastavam usred sinova Izrailjevijeh.

< Numeri 35 >