< Numeri 32 >

1 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
A sinovi Ruvimovi i sinovi Gadovi imahu vrlo mnogo stoke, i vidješe zemlju Jazirsku i zemlju Galadsku da je dobra za stoku.
2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
I došavši sinovi Gadovi i sinovi Ruvimovi rekoše Mojsiju i Eleazaru svešteniku i knezovima od zbora govoreæi:
3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
Atarot i Devon i Jazir i Namra i Esevon i Elealija i Sevama i Navav i Vean,
4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
Ta je zemlja, koju Gospod pokori zboru Izrailjskom, dobra za stoku, a sluge tvoje imaju stoke.
5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
Ako smo, rekoše, našli milost pred tobom, neka se ta zemlja dade slugama tvojim u našljedstvo, nemoj nas voditi preko Jordana.
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
A Mojsije reèe sinovima Gadovijem i sinovima Ruvimovijem: braæa æe vaša iæi na vojsku, a vi hoæete ovdje da ostanete?
7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
Zašto obarate srce sinovima Izrailjevijem da ne prijeðu u zemlju koju im je dao Gospod?
8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
Tako su uèinili oci vaši, kad ih poslah iz Kadis-Varne da uhode zemlju;
9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
I otidoše do potoka Eshola, i uhodiše zemlju; i oboriše srce sinovima Izrailjevijem da ne idu u zemlju koju im dade Gospod;
10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
I razgnjevi se onda Gospod, i zakle se govoreæi:
11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Neæe ti ljudi koji izaðoše iz Misira, od dvadeset godina i više, vidjeti zemlje za koju se zakleh Avramu, Isaku i Jakovu, jer se ne držaše mene sasvijem,
12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
Osim Haleva sina Jefonijina Kenezeja i Isusa sina Navina, jer se sasvijem držaše Gospoda.
13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
I razgnjevi se Gospod na Izrailja, i uèini te se potucaše po pustinji èetrdeset godina, dokle ne pomrije sav onaj naraštaj koji èinjaše zlo pred Gospodom.
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
A vi sada izaðoste na mjesto otaca svojih, rod griješnih ljudi, da umnožavate žestinu gnjeva Gospodnjega na Izrailja.
15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
Ako se odvratite od njega, on æe ga još ostaviti u pustinji, i tako æete upropastiti sav onaj narod.
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
A oni pristupiše opet k njemu, i rekoše mu: mi smo radi samo torove naèiniti ovdje za stada svoja i gradove za djecu svoju.
17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
A sami æemo naoružani junaèki poæi pred sinovima Izrailjevijem, dokle ih ne odvedemo na njihovo mjesto; a naša djeca neka stoje u gradovima tvrdijem radi stanovnika te zemlje.
18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
Neæemo se vratiti kuæama svojim dokle sinovi Izrailjevi ne prime svaki svoje našljedstvo.
19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
Niti æemo uzeti našljedstva s njima s onu stranu Jordana ni dalje, ako nam dopadne našljedstvo s ovu stranu Jordana prema istoku.
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
Tada im reèe Mojsije: ako æete uèiniti tako i iæi pod oružjem pred Gospodom na vojsku,
21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
Ako svaki od vas pod oružjem prijeðe preko Jordana pred Gospodom, dokle ne otjera ispred sebe neprijatelja svojih,
22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
I dokle se ne pokori zemlja pred Gospodom, pa se onda vratite i ne zgriješite Gospodu ni Izrailju, onda æe ova zemlja pripasti vama u našljedstvo pred Gospodom.
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
Ako li ne uèinite tako, gle, zgriješiæete Gospodu, i znajte da æe vas grijeh vaš stiæi.
24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
Gradite sebi gradove za djecu svoju i torove za stoku svoju; i što je izašlo iz usta vaših, uèinite.
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
I rekoše Mojsiju sinovi Gadovi i sinovi Ruvimovi govoreæi: sluge æe tvoje uèiniti kako gospodar naš zapovijeda.
26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
Djeca naša i žene naše, stada naša i sva stoka naša ovdje æe ostati u gradovima Galadskim;
27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
A sluge æe tvoje prijeæi svaki naoružan, da se bije pred Gospodom, kao što govori gospodar naš.
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
Tada Mojsije zapovjedi za njih Eleazaru svešteniku i Isusu sinu Navinu i glavarima od domova otaèkih meðu sinovima Izrailjevijem,
29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
I reèe im: ako prijeðu sinovi Gadovi i sinovi Ruvimovi s vama preko Jordana, svi oružani, da se biju pred Gospodom, i kad vam bude zemlja pokorena, onda podajte njima zemlju Galadsku u našljedstvo.
30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
Ako li ne prijeðu s vama pod oružjem, onda neka im bude našljedstvo meðu vama u zemlji Hananskoj.
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
I odgovoriše sinovi Gadovi i sinovi Ruvimovi govoreæi: kako je Gospod kazao slugama tvojim tako æemo uèiniti.
32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
Prijeæi æemo pod oružjem pred Gospodom u zemlju Hanansku, a naše našljedstvo da bude s ovu stranu Jordana.
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
I dade Mojsije sinovima Gadovijem i sinovima Ruvimovijem i polovini plemena Manasije sina Josifova carstvo Siona cara Amorejskoga i carstvo Oga cara Vasanskoga, zemlju i gradove po meðama njezinijem, gradove one zemlje unaokolo.
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
I sagradiše sinovi Gadovi Devon i Atarot i Aroir.
35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
I Atrot-Sofan i Jazir i Jogveju,
36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
I Vet-Nimru i Vet-Aran, gradove tvrde, i torove za stoku.
37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
A sinovi Ruvimovi sagradiše Esevon i Elealiju i Kirijatajim,
38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
I Navon i Velmeon predjenuvši im imena, i Sivmu; i nadješe druga imena gradovima koje sagradiše.
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
A sinovi Mahira sina Manasijina otidoše u Galad, i uzeše ga, i izagnaše Amoreje koji bijahu ondje.
40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
I Mojsije dade Galad Mahiru sinu Manasijinu, koji se ondje naseli.
41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
I Jair sin Manasijin otide i uze sela njihova i prozva ih sela Jairova.
42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
I Navav otide i uze Kenat sa selima njegovijem, i prozva ga Navav po imenu svojemu.

< Numeri 32 >